-
Levitiko 22:18-20Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
18 “Uza Aroni ndi ana ake komanso Aisiraeli onse kuti, ‘Mwamuna aliyense amene ndi wa Chiisiraeli kapena mlendo wokhala mu Isiraeli amene akupereka kwa Yehova nsembe yopsereza+ pofuna kukwaniritsa malonjezo ake kapena kuti ikhale nsembe yake yaufulu,+ 19 azipereka nyama yopanda chilema,+ ngʼombe zamphongo, nkhosa zamphongo kapena mbuzi, kuti Mulungu asangalale naye. 20 Musamapereke nsembe nyama iliyonse yachilema,+ chifukwa Mulungu sangasangalale nanu.
-