Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 12:5, 6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Mʼmalomwake, mudzafunefune Yehova Mulungu wanu pamalo alionse amene adzasankhe kuti aikepo dzina lake komanso malo amene azidzakhala pakati pa mafuko anu onse, ndipo muzidzapita kumeneko.+ 6 Nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zina, zopereka zanu za chakhumi,*+ chopereka chochokera mʼmanja mwanu,+ nsembe zimene mukupereka pokwaniritsa lonjezo, nsembe zanu zaufulu,+ ana oyamba kubadwa a ngʼombe ndi a nkhosa zanu,+ zonsezi muzidzapita nazo kumalo amenewo.+

  • Deuteronomo 14:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Muzidzadya chakhumi cha mbewu zanu, kumwa vinyo wanu watsopano, kudya mafuta anu, ana oyamba a ngʼombe ndi a nkhosa zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu, pamalo amene iye adzasankhe kuikapo dzina lake.+ Muzidzachita zimenezi kuti mudzaphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu nthawi zonse.+

  • Deuteronomo 16:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Ndipo muzidzasangalala pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inuyo, mwana wanu wamwamuna, mwana wanu wamkazi, kapolo wanu wamwamuna, kapolo wanu wamkazi, Mlevi amene akukhala mumzinda wanu,* mlendo amene akukhala pakati panu, mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye, amene ali pakati panu. Muzidzasangalala pamalo amene Yehova Mulungu wanu adzasankhe kuikapo dzina lake.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena