Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Samueli 5:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Kale, pamene Sauli anali mfumu yathu, inuyo ndi amene munkatsogolera Aisiraeli kunkhondo.*+ Ndipo Yehova anakuuzani kuti, ‘Udzaweta anthu anga Aisiraeli ndipo udzakhala mtsogoleri wa Aisiraeli.’”+

  • 1 Mbiri 17:7-10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Tsopano mtumiki wanga Davide ukamuuze kuti, ‘Yehova wa magulu ankhondo akumwamba wanena kuti: “Ine ndinakutenga kubusa kumene unkaweta nkhosa kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisiraeli.+ 8 Ine ndidzakhala nawe kulikonse kumene ungapite+ ndipo ndidzagonjetsa adani ako onse pamaso pako.+ Ndidzachititsa kuti dzina lako lidziwike ngati mmene zimakhalira ndi anthu otchuka mʼdzikoli.+ 9 Anthu anga Aisiraeli ndidzawasankhira malo nʼkuwakhazika pamalowo. Iwo adzakhala pamenepo ndipo sadzasokonezedwanso. Anthu oipa sadzawaponderezanso ngati mmene ankachitira kale,+ 10 pa nthawi imene ndinasankha oweruza kuti azitsogolera anthu anga Aisiraeli.+ Ndipo ndidzagonjetsa adani ako onse.+ Kuwonjezera pamenepo, ndikukuuza kuti: ‘Yehova adzakumangira nyumba.’*

  • 1 Mbiri 28:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Komabe, mʼnyumba yonse ya bambo anga Yehova Mulungu wa Isiraeli anasankha ineyo kuti ndikhale mfumu ya Isiraeli mpaka kalekale,+ chifukwa anasankha Yuda kuti akhale mtsogoleri.+ Mʼnyumba ya Yuda anasankhamo nyumba ya bambo anga.+ Pa ana a bambo anga anavomereza ineyo kuti ndikhale mfumu ya Aisiraeli onse.+

  • Salimo 78:70, 71
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 70 Anasankha Davide+ mtumiki wake,

      Ndipo anamuchotsa kumakola a nkhosa,+

      71 Kumene ankaweta nkhosa zoyamwitsa,

      Anamuika kuti akhale mʼbusa wa ana a Yakobo, omwe ndi anthu ake,+

      Ndi Isiraeli, amene ndi cholowa chake.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena