-
Danieli 4:34, 35Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
34 “Nthawi imeneyi itatha,+ ine Nebukadinezara ndinayangʼana kumwamba ndipo nzeru zanga zinabwerera. Ndinatamanda Wamʼmwambamwamba ndipo amene adzakhalepo mpaka kalekale ndinamutamanda ndi kumulemekeza, chifukwa ulamuliro wake udzakhalapo mpaka kalekale ndipo ufumu wake udzakhalapo kumibadwomibadwo.+ 35 Anthu onse okhala padziko lapansi ndi opanda pake poyerekezera ndi Mulungu. Iye amachita zinthu mogwirizana ndi zofuna zake pakati pa magulu akumwamba ndi anthu okhala padziko lapansi. Palibe aliyense amene angamulepheretse kuchita zimene akufuna+ kapena kumufunsa kuti, ‘Mukuchita chiyani?’+
-