Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 4:9, 10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Pambuyo pake, Yehova anafunsa Kaini kuti: “Kodi mʼbale wako Abele ali kuti?” Iye anayankha kuti: “Sindikudziwa. Kodi ndine mlonda wa mʼbale wangayo?” 10 Pamenepo Mulungu anati: “Nʼchiyani chimene wachitachi? Tamvetsera, magazi a mʼbale wako akundilirira munthaka.+

  • Genesis 9:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Kuwonjezera pamenepo, aliyense amene adzakupheni* ndidzamupatsa chilango. Ngati chamoyo chilichonse chapha munthu, chamoyocho chidzaphedwanso. Ndipo munthu aliyense wochotsa moyo wa mʼbale wake, ndidzamupatsa chilango.+

  • Deuteronomo 32:43
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 43 Inu anthu a mitundu ina, sangalalani limodzi ndi anthu ake,+

      Chifukwa adzabwezera magazi a atumiki ake,+

      Ndipo adzabwezera chilango kwa adani ake,+

      Komanso adzaphimba machimo a dziko la anthu ake.”*

  • 2 Mafumu 9:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Zitatero Yehu anakoka uta wake nʼkubaya Yehoramu kumsana pakati pamapewa mpaka muviwo unatulukira pamtima pake ndipo Yehoramu anagwa mʼgaleta lake lankhondo.

  • 2 Mafumu 9:26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 ‘Yehova wanena kuti: “Ndithu magazi a Naboti+ ndi magazi a ana ake amene ndawaona dzulo, ndidzawabwezera+ pa iwe mʼmunda uwu,” watero Yehova.’ Choncho munyamule umuponye mʼmundamo mogwirizana ndi mawu a Yehova.”+

  • 2 Mafumu 24:3, 4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Zimenezi zinachitikira Ayuda molamulidwa ndi Yehova, kuti awachotse pamaso pake+ chifukwa cha machimo onse amene Manase anachita+ 4 komanso chifukwa cha anthu ambiri osalakwa amene anawapha,+ moti anadzaza Yerusalemu ndi magazi a anthu osalakwa ndipo Yehova sanafune kukhululuka.+

  • Luka 11:49-51
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 49 Nʼchifukwa chake nzeru ya Mulungu inanenanso kuti: ‘Ndidzawatumizira aneneri ndi atumwi, koma iwo adzapha komanso kuzunza ena mwa iwo. 50 Choncho mʼbadwo uwu udzaimbidwa mlandu wa magazi a aneneri, amene anakhetsedwa kuyambira pamene dziko linakhazikika.+ 51 Kuyambira magazi a Abele+ mpaka magazi a Zekariya, amene anaphedwa pakati pa guwa lansembe ndi nyumba yopatulika.’*+ Inde ndikukuuzani, mʼbadwo uwu udzayankha mlandu wa magazi amenewo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena