-
Deuteronomo 6:10-12Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
10 Ndiyeno Yehova Mulungu wanu akadzakulowetsani mʼdziko limene analumbira kwa makolo anu Abulahamu, Isaki ndi Yakobo kuti adzakupatsani,+ dziko lokhala ndi mizinda ikuluikulu yabwino imene simunamange ndinu,+ 11 yokhalanso ndi nyumba zodzaza ndi zinthu zosiyanasiyana zabwino zimene simunagwirire ntchito, zitsime zimene simunakumbe ndinu komanso minda ya mpesa ndi mitengo ya maolivi imene simunadzale ndinu, ndiye mukakadya nʼkukhuta,+ 12 mukasamale kuti musakaiwale Yehova+ amene anakutulutsani mʼdziko la Iguputo, mʼnyumba yaukapolo.
-
-
Yobu 31:28Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
28 Chimenecho chikanakhala cholakwa chimene oweruza akuyenera kundipatsira chilango,
Chifukwa ndikanakhala nditakana Mulungu woona wakumwamba.
-