Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yobu 34:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Chifukwa iye amapereka mphoto kwa munthu mogwirizana ndi zimene amachita,+

      Ndipo amamusiya kuti akumane ndi mavuto chifukwa cha zochita zake.

  • Miyambo 24:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Ukanena kuti: “Ifetu zimenezi sitimazidziwa,”

      Kodi amene amafufuza mitima sazindikira zimene zili mʼmaganizo mwako?+

      Ndithudi, amene amakuyangʼanitsitsa adzadziwa

      Ndipo adzabwezera munthu aliyense mogwirizana ndi zochita zake.+

  • Aroma 2:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Iye adzaweruza aliyense mogwirizana ndi zochita zake.+

  • 2 Akorinto 5:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Chifukwa aliyense wa ife adzaonekera kumpando woweruzira milandu wa Khristu, kuti alandire mphoto yake mogwirizana ndi zimene anachita ali mʼthupi, kaya zabwino kapena zoipa.+

  • Agalatiya 6:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Musadzinamize, Mulungu sapusitsika. Chilichonse chimene munthu wafesa, adzakololanso chomwecho.+

  • 2 Timoteyo 4:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Alekizanda wosula zinthu zakopa uja, anandichitira zoipa kwambiri. Yehova* adzamubwezera mogwirizana ndi ntchito zake.+

  • Chivumbulutso 20:12, 13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Ndiye ndinaona akufa, olemekezeka ndi onyozeka, ataimirira pamaso pa mpando wachifumuwo, ndipo mipukutu inatambasulidwa. Koma panali mpukutu wina umene unatambasulidwa, womwe ndi mpukutu wa moyo.+ Akufa anaweruzidwa potengera zimene zinalembedwa mʼmipukutuyo, mogwirizana ndi ntchito zawo.+ 13 Nyanja inapereka akufa amene anali mmenemo. Imfa komanso Manda* zinapereka akufa amene anali mmenemo. Aliyense payekha anaweruzidwa mogwirizana ndi ntchito zake.+

  • Chivumbulutso 22:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 ‘Taonani! Ndikubwera mofulumira ndipo ndili ndi mphoto yoti ndipereke kwa aliyense mogwirizana ndi ntchito yake.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena