19 Dzuwa silidzakhalanso lokuunikira masana,
Ndipo mwezi sudzakuunikiranso.
Chifukwa Yehova adzakhala kuwala kwako mpaka kalekale,+
Ndipo Mulungu wako adzakhala kukongola kwako.+
20 Dzuwa lako silidzalowanso,
Ndipo mwezi wako sudzasiya kuwala,
Chifukwa Yehova adzakhala kuwala kwako mpaka kalekale,+
Ndipo masiku ako olira adzakhala atatha.+