Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 15:7, 8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Ngati mmodzi mwa abale anu wasauka pakati panu, mu umodzi mwa mizinda yanu mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musamamuumire mtima kapena kumuumitsira dzanja lanu.+ 8 Koma muzithandiza mʼbale wanuyo mowolowa manja,+ ndipo mulimonse mmene zingakhalire, muzimukongoza* chilichonse chimene akufuna kapena chimene akusowa.

  • Salimo 41:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 41 Wosangalala ndi munthu amene amachita zinthu moganizira munthu wonyozeka.+

      Pa tsiku la tsoka, Yehova adzamupulumutsa.

  • Miyambo 19:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Amene amakomera mtima munthu wonyozeka akukongoza Yehova,+

      Ndipo adzamʼbwezera* zimene anachitazo.+

  • Luka 6:34, 35
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Komanso, ngati mumakongoza popanda chiwongoladzanja kwa okhawo amene mukuyembekezera kuti adzabweza ngongoleyo, mudzapindula chiyani?+ Ochimwanso amakongoza ochimwa anzawo popanda chiwongoladzanja, kuti adzawabwezere zomwezo. 35 Mosiyana ndi zimenezo, inu pitirizani kukonda adani anu. Pitirizani kuchita zabwino ndi kukongoza popanda chiwongoladzanja, osayembekezera kulandira kalikonse.+ Mukatero, mphoto yanu idzakhala yaikulu ndipo mudzakhala ana a Wamʼmwambamwamba, chifukwa iye ndi wokoma mtima kwa osayamika ndi kwa oipa.+

  • Machitidwe 20:35
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 35 Pa zinthu zonse ndakusonyezani kuti pogwira ntchito molimbikira chonchi,+ muzithandiza ofooka ndipo muzikumbukira mawu a Ambuye Yesu. Paja iye anati, ‘Kupatsa kumatichititsa kukhala osangalala kwambiri+ kuposa kulandira.’”

  • Aheberi 13:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Komanso musaiwale kuchita zabwino ndi kugawira ena zomwe muli nazo,+ chifukwa Mulungu amasangalala ndi nsembe zoterozo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena