15 Chifukwa Wapamwamba ndi Wokwezeka,
Amene adzakhalepo mpaka kalekale+ ndiponso dzina lake ndi loyera,+ wanena kuti:
“Ine ndimakhala pamalo apamwamba komanso oyera,+
Koma ndimakhalanso ndi anthu opsinjika ndiponso amene ali ndi mtima wodzichepetsa,
Kuti nditsitsimutse mtima wa anthu onyozeka
Ndiponso kuti nditsitsimutse mtima wa anthu opsinjika.+