Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Samueli 15:22, 23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Samueli anati: “Kodi Yehova amasangalala ndi nsembe zopsereza ndi nsembe zina+ kuposa kumvera mawu a Yehova? Dikira ndikuuze! Kumvera kumaposa nsembe,+ ndipo kumvetsera mosamala kumaposa mafuta+ a nkhosa zamphongo. 23 Chifukwa kupanduka+ nʼchimodzimodzi ndi tchimo la kuwombeza,+ ndipo kuchita zinthu modzikuza nʼchimodzimodzi ndi kugwiritsa ntchito mphamvu zamatsenga ndiponso kulambira mafano.* Popeza wakana mawu a Yehova,+ iyenso wakukana kuti ukhale mfumu.”+

  • Hoseya 6:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  6 Chifukwa ndimakondwera ndi chikondi chokhulupirika,* osati nsembe.

      Ndimakondweranso ndi kudziwa Mulungu, osati nsembe zopsereza zathunthu.+

  • Mika 6:7, 8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  7 Kodi Yehova adzasangalala ndi masauzande a nkhosa zamphongo?

      Kodi adzakondwera ndi mitsinje ya mafuta masauzande ambirimbiri?+

      Kodi ndipereke mwana wanga wamwamuna woyamba chifukwa cha zolakwa zanga,

      Ndipereke chipatso cha mimba yanga chifukwa cha tchimo langa?+

       8 Iye anakuuza munthu iwe zimene zili zabwino.

      Kodi Yehova akufuna kuti uzichita* chiyani?

      Iye akungofuna kuti uzichita chilungamo,*+ uziona kuti kukhulupirika nʼkofunika,*+

      Ndiponso uziyenda modzichepetsa+ ndi Mulungu wako.+

  • Mateyu 12:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Komabe, ngati mukanamvetsa tanthauzo la mawu akuti, ‘Ndikufuna chifundo+ osati nsembe,’+ simukanaweruza anthu osalakwa.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena