Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 4:29
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 29 Mukadzafufuza Yehova Mulungu wanu muli kumeneko, mukadzamufunafuna ndi mtima wanu wonse komanso moyo wanu wonse, mudzamupezadi.+

  • Deuteronomo 30:1-4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 30 “Mawu onsewa akadzakwaniritsidwa pa inu, madalitso ndi matemberero amene ndaika pamaso panu,+ ndipo mukadzawakumbukira*+ muli ku mitundu yonse kumene Yehova Mulungu wanu adzakubalalitsireni,+ 2 inu nʼkubwerera kwa Yehova Mulungu wanu+ komanso kumvera mawu ake ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, mogwirizana ndi zonse zimene ndikukulamulani lero, inuyo ndi ana anu,+ 3 Yehova Mulungu wanu adzabweza kwawo anthu a mtundu wanu amene anagwidwa nʼkupita kudziko lina,+ ndipo adzakuchitirani chifundo+ nʼkukusonkhanitsaninso pamodzi kuchokera pakati pa anthu onse kumene Yehova Mulungu wanu anakubalalitsirani.+ 4 Ngakhale anthu a mtundu wanu amene anabalalitsidwawo atadzakhala kumalekezero kwa thambo, Yehova Mulungu wanu adzakusonkhanitsani nʼkukubweretsani kuchokera kumeneko.+

  • 1 Mafumu 8:47, 48
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 47 ndiyeno iwo nʼkuzindikira kulakwa kwawo mʼdziko limene anawatengeralo+ nʼkulapa,+ ndiponso akapempha chifundo kwa inu mʼdziko la adani awowo+ nʼkunena kuti, ‘Tachimwa, talakwitsa ndiponso tachita zinthu zoipa,’+ 48 nʼkubwerera kwa inu ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse,+ mʼdziko la adani awo amene anawagwira ndiponso akapemphera kwa inu atayangʼana kudziko lawo limene munapatsa makolo awo, mzinda umene mwasankha komanso nyumba ya dzina lanu imene ndamanga,+

  • Yeremiya 24:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Ndidzawapatsa mtima woti andidziwe kuti ine ndine Yehova.+ Iwo adzakhala anthu anga ndipo ine ndidzakhala Mulungu wawo+ chifukwa adzabwerera kwa ine ndi mtima wawo wonse.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena