Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 15:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Chilichonse chomwe amachita pondilambira ndi chopanda pake, chifukwa amaphunzitsa malamulo a anthu ngati kuti ndi malamulo a Mulungu.’”+

  • Maliko 7:8-13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Mumanyalanyaza malamulo a Mulungu nʼkumaumirira miyambo ya anthu.”+

      9 Komanso anawauza kuti: “Mochenjera, mumanyalanyaza malamulo a Mulungu kuti musunge miyambo yanu.+ 10 Mwachitsanzo, Mose ananena kuti, ‘Muzilemekeza bambo anu ndi mayi anu,’+ komanso anati, ‘Aliyense wolankhula mawu achipongwe kwa bambo ake kapena mayi ake aziphedwa.’+ 11 Koma inu mumanena kuti, ‘Munthu akauza bambo ake kapena mayi ake kuti: “Chilichonse chimene ndili nacho, chimene ndikanakuthandizani nacho ndi khobani (kutanthauza, mphatso yoti ndipereke kwa Mulungu),”’ 12 inu simulolanso kuti munthuyo achitire bambo ake kapena mayi ake chinthu chilichonse.+ 13 Mukamachita zimenezi, mumapangitsa kuti mawu a Mulungu akhale opanda pake chifukwa cha miyambo yanu imene munaipereka kwa anthu.+ Ndipo mumachita zinthu zambiri ngati zimenezi.”+

  • Akolose 2:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Samalani kuti wina asakugwireni ukapolo,* pogwiritsa ntchito nzeru za anthu ndi chinyengo chopanda pake,+ mogwirizana ndi miyambo ya anthu komanso mfundo zimene anthu amʼdzikoli amayendera, osati mogwirizana ndi Khristu,

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena