-
Maliko 12:35-37Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
35 Komabe, pamene Yesu ankaphunzitsa mʼkachisi, ananena kuti: “Nʼchifukwa chiyani alembi amanena kuti Khristu ndi mwana wa Davide?+ 36 Kudzera mwa mzimu woyera,+ Davideyo ananena kuti, ‘Yehova* anauza Ambuye wanga kuti: “Khala kudzanja langa lamanja mpaka nditaika adani ako pansi pa mapazi ako.”’+ 37 Davideyo anamutchula kuti Ambuye, ndiye zingatheke bwanji kuti akhale mwana wake?”+
Ndipo gulu lalikulu la anthu linkamumvetsera mosangalala.
-
-
Luka 20:41-44Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
41 Ndiyeno iye anawafunsa kuti: “Nʼchifukwa chiyani amanena kuti Khristu ndi mwana wa Davide?+ 42 Chifukwa Davideyo ananena mʼbuku la Masalimo kuti, ‘Yehova* anauza Ambuye wanga kuti: “Khala kudzanja langa lamanja 43 mpaka nditaika adani ako kuti akhale chopondapo mapazi ako.”’+ 44 Choncho Davide anamutchula kuti Ambuye. Ndiye zikutheka bwanji kuti akhale mwana wake?”
-