Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Maliko 14:37-42
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 37 Atatero anabwerera ndipo anawapeza akugona. Choncho anafunsa Petulo kuti: “Simoni, zoona ukugona? Kodi unalibe mphamvu kuti ukanakhalabe maso kwa ola limodzi?+ 38 Khalani maso ndipo mupitirize kupemphera kuti musalowe mʼmayesero.+ Zoona, mzimu ndi wofunitsitsa, koma thupi ndi lofooka.”+ 39 Atatero anachokanso kupita kukapemphera ndipo ananenanso mawu omwe aja.+ 40 Anabweranso nʼkuwapeza akugona, chifukwa zikope zawo zinali zitalemera, choncho iwo anasowa chomuyankha. 41 Anabweranso kachitatu nʼkuwauza kuti: “Zoona nthawi ngati ino mukugona ndi kupumula? Basi! Nthawi yakwana!+ Taonani! Mwana wa munthu akuperekedwa mʼmanja mwa anthu ochimwa. 42 Nyamukani, tiyeni tizipita. Onani! Wondipereka uja ali pafupi.”+

  • Luka 22:45
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 45 Atanyamuka pamene amapempherapo nʼkupita kwa ophunzira aja, anawapeza atagona chifukwa anali atafooka ndi chisoni.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena