-
Maliko 14:60-65Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
60 Kenako, mkulu wa ansembe anaimirira pakati pawo nʼkufunsa Yesu kuti: “Kodi suyankha? Kodi sukumva zimene anthuwa akukunenezazi?”+ 61 Koma iye anangokhala chete osayankha chilichonse.+ Apanso mkulu wa ansembe anayamba kumufunsa kuti: “Kodi ndiwe Khristu Mwana wa Wodalitsidwayo?” 62 Ndiyeno Yesu ananena kuti: “Inde ndinedi, ndipo mudzaona Mwana wa munthu+ atakhala kudzanja lamanja+ lamphamvu. Mudzamuonanso akubwera ndi mitambo yakumwamba.”+ 63 Mkulu wa ansembe atamva zimenezi anangʼamba zovala zake nʼkunena kuti: “Nanga tingafunenso mboni zina pamenepa?+ 64 Mwadzimvera nokha mmene akunyozera Mulungu. Mukuona bwanji pamenepa?”* Onse ananena kuti akuyenera kufa basi.+ 65 Ndipo ena anayamba kumulavulira,+ kumuphimba nkhope nʼkumamukhoma nkhonya. Iwo ankamuuza kuti: “Losera!” Atamuwomba mbama, asilikali apakhoti anamutenga.+
-