Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 22:23-28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Pa tsiku limenelo Asaduki amene amanena kuti akufa sadzaukitsidwa,+ anabwera nʼkumufunsa kuti:+ 24 “Mphunzitsi, Mose ananena kuti: ‘Ngati mwamuna wamwalira asanabereke ana, mchimwene wake akuyenera kukwatira mkazi wamasiyeyo nʼkuberekera mchimwene wake uja ana.’+ 25 Tsopano panali amuna 7 apachibale. Woyamba anakwatira kenako nʼkumwalira. Koma popeza kuti analibe ana, mkaziyo anakwatiwa ndi mchimwene wa mwamuna wake uja. 26 Zinachitika chimodzimodzi kwa wachiwiri ndi wachitatu, mpaka kwa onse 7 aja. 27 Pamapeto pake mkazi uja anamwaliranso. 28 Kodi pamenepa, akufa akadzaukitsidwa mkazi ameneyu adzakhala wa ndani? Popeza onse 7 anamukwatira.”

  • Luka 20:27-33
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Koma Asaduki ena, amene amanena kuti akufa sadzaukitsidwa,+ anabwera nʼkumufunsa kuti:+ 28 “Mphunzitsi, Mose anatilembera kuti, ‘Ngati mwamuna wamwalira nʼkusiya mkazi koma sanabereke ana, mchimwene wake akuyenera kutenga mkazi wamasiyeyo nʼkuberekera mchimwene wake uja ana.’+ 29 Ndiyeno panali amuna 7 apachibale. Woyamba anakwatira mkazi, koma anamwalira asanabereke mwana. 30 Wachiwirinso chimodzimodzi. 31 Kenako wachitatu anamukwatira. Zinachitika chimodzimodzi kwa amuna onse 7 aja, onse anamwalira osasiya ana. 32 Pamapeto pake mkazi uja anamwaliranso. 33 Kodi pamenepa, akufa akadzaukitsidwa mkazi ameneyu adzakhala wa ndani? Popeza onse 7 anamukwatira.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena