-
Mateyu 27:27-31Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
27 Ndiyeno asilikali a bwanamkubwa anatenga Yesu nʼkulowa naye mʼnyumba ya bwanamkubwayo ndipo anasonkhanitsa gulu lonse la asilikali kwa iye.+ 28 Kumeneko anamuvula zovala zake nʼkumuveka chinsalu chofiira kwambiri.+ 29 Komanso analuka chisoti chachifumu chaminga nʼkumuveka kumutu ndipo anamupatsa bango mʼdzanja lake lamanja. Kenako anamugwadira nʼkumamunyoza kuti: “Moni, inu Mfumu ya Ayuda!” 30 Atatero anamulavulira+ ndipo anatenga bango lija nʼkuyamba kumumenya nalo mʼmutu. 31 Atamaliza kumunyozako, anamuvula chinsalu chija nʼkumuveka malaya ake akunja ndipo anapita naye kuti akamukhomerere pamtengo.+
-