Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 10:2-4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Mayina a atumwi 12 ndi awa:+ Simoni, amene ankatchulidwa kuti Petulo*+ ndi Andireya+ mchimwene wake. Yakobo mwana wa Zebedayo ndi mchimwene wake Yohane.+ 3 Filipo ndi Batolomeyo,+ Tomasi+ ndi Mateyu+ wokhometsa msonkho, Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Tadeyo. 4 Simoni Kananiya* ndi Yudasi Isikariyoti, amene pambuyo pake anapereka Yesu.+

  • Maliko 3:14-19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Ndiyeno anasankha gulu la anthu 12, amenenso anawapatsa dzina lakuti atumwi, kuti aziyenda naye nthawi zonse komanso kuti aziwatuma kukalalikira 15 nʼkuwapatsa mphamvu zoti azitulutsa ziwanda.+

      16 Mʼgulu la anthu 12+ amene anasankha aja munali Simoni, amene anamupatsanso dzina lakuti Petulo,+ 17 Yakobo mwana wa Zebedayo ndi Yohane mchimwene wake wa Yakobo (awiriwa anawapatsanso dzina lakuti Boanege, limene limatanthauza “Ana a Bingu”),+ 18 Andireya, Filipo, Batolomeyo, Mateyu, Tomasi, Yakobo mwana wa Alifeyo, Tadeyo, Simoni Kananiya,* 19 ndi Yudasi Isikariyoti, amene pambuyo pake anadzamʼpereka.

      Kenako Yesu analowa mʼnyumba.

  • Machitidwe 1:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Atafika mumzindawo anapita mʼchipinda chamʼmwamba, mmene ankakhala. Panali Petulo, Yohane, Yakobo, Andireya, Filipo, Tomasi, Batolomeyo, Mateyu, Yakobo mwana wa Alifeyo, Simoni wodzipereka uja komanso Yudasi mwana wa Yakobo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena