Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Salimo 22:16-18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Adani anga andizungulira ngati agalu.+

      Andizungulira ngati gulu la anthu ochita zoipa,+

      Mofanana ndi mkango, iwo akundiluma manja ndi mapazi.+

      17 Ndingathe kuwerenga mafupa anga onse.+

      Adaniwo akuona zimenezi ndipo akundiyangʼanitsitsa.

      18 Iwo akugawana zovala zanga,

      Ndipo akuchita maere pa zovala zanga.+

  • Yesaya 53:7-9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  7 Iye anachitiridwa zankhanza+ ndipo analola kuti azunzidwe,+

      Koma sanatsegule pakamwa pake.

      Anamutengera kumalo oti akamuphere ngati nkhosa,+

      Mofanana ndi nkhosa yaikazi imene yangokhala chete pamene akufuna kuimeta ubweya,

      Ndipo sanatsegule pakamwa pake.+

       8 Iye anaponderezedwa ndipo anatengedwa popanda kuweruzidwa mwachilungamo.

      Ndi ndani amene anaganizira tsatanetsatane wa mʼbadwo wa makolo ake?*

      Popeza iye anadulidwa mʼdziko la anthu amoyo.+

      Iye anakwapulidwa* chifukwa cha zolakwa za anthu anga.+

       9 Anapatsidwa manda* limodzi ndi anthu oipa,+

      Ndipo pamene anafa anaikidwa mʼmanda limodzi ndi anthu olemera,*+

      Ngakhale kuti iye sanalakwe chilichonse*

      Ndipo mʼkamwa mwake munalibe chinyengo.+

  • 1 Akorinto 15:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Pa zinthu zoyambirira zimene ndinakuphunzitsani, zomwenso ineyo ndinalandira, panali zonena kuti, Khristu anafera machimo athu, mogwirizana ndi Malemba.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena