13 Lowani pageti lalingʼono.+ Chifukwa msewu umene ukupita kuchiwonongeko ndi wotakasuka komanso geti lake ndi lalikulu ndipo anthu ambiri akudzera pageti limenelo. 14 Koma geti lolowera ku moyo ndi lalingʼono komanso msewu wake ndi wopanikiza ndipo amene akuupeza ndi ochepa.+