Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gl tsamba 32-33
  • Chikristu Chifalikira Kumayiko Ena

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chikristu Chifalikira Kumayiko Ena
  • ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Nkhani Yofanana
  • Maufumu Athira Nkhondo Dziko Lolonjezedwa
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Mayiko Otchulidwa M’baibulo
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Girisi ndi Roma Akhudza Moyo wa Ayuda
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Anthu a Mulungu Abwerera Kudziko Lawo
    ‘Onani Dziko Lokoma’
Onani Zambiri
‘Onani Dziko Lokoma’
gl tsamba 32-33

Chikristu Chifalikira Kumayiko Ena

YESU pa Phiri la Azitona pafupi ndi Betaniya, analamula zogwira ntchito yolalikira yomwe ikasintha mbiri ya dziko lonse. Ntchito imeneyi ikayambira ku Yerusalemu, pafupifupi makilomita atatu kumadzulo. Uthengawo ukafalikira kumadera apafupi a Yudeya ndi Samariya, mpaka “kufikira ku malekezero ake a dziko.”—Mac. 1:4, 8, 12.

Patangopita nthaŵi yochepa Yesu atanena mawu ameneŵa, Phwando la Pentekoste linasonkhanitsa Ayuda ndi anthu oloŵa Chiyuda ochokera m’madera onse a Ufumu wa Roma, osonyezedwa pamapu ali m’munsiŵa. Chikristu chinafalikira kwambiri pamene mtumwi Petro analalikira kwa anthuwo tsiku limenelo.—Mac. 2:9-11.

Kufalikira kwa Chikhristu

Posapita nthaŵi, chizunzo chinabalalitsa otsatira a Kristu kuchoka m’Yerusalemu. Petro ndi Yohane anathandiza Asamariya kumvetsa komanso kulandira uthenga wabwino. (Mac. 8:1, 4, 14-16) Chikristu chinafalikira ku Africa pamene Filipo analalikira Mwaitiopiya m’njira ya m’chipululu ‘yochokera ku Yerusalemu kumka ku Gaza.’ (Mac. 8:26-39) Inali nthaŵi yomweyo pamene uthenga wabwino unabala zipatso m’dera la Luda, lomwe lili ku Chigwa cha Saroni, ku doko la Yopa. (Mac. 9:35, 42) Kenako Petro anapita ku Kaisareya kumene anathandiza Korneliyo, yemwe anali ofesala wa Roma, ndi abale ake, ndiponso anzake kukhala Akristu odzozedwa ndi mzimu.—Mac. 10:1-48.

Maulendo A Paulo

Paulo, yemwe poyamba anali kuzunza Akristu, anadzakhala mtumwi wa kwa anthu amitundu. Pamaulendo ake onse atatu aumishonale, ndi ulendo wake womaliza wopita ku Roma, Paulo anayenda pamtunda ndi pasitima za pamadzi. Mtumwiyu ndi anthu ena anafalitsa uthenga wabwino ku mizinda yambiri ya Ufumu wa Roma. Paulo anafunitsitsa kukafika ku Spanya (Onani patsamba 2.), ndipo Petro anakatumikira mpaka kum’maŵa kwenikweni, ku Babulo. (1 Pet. 5:13) Inde, chifukwa cha utsogoleri wamphamvu wa Kristu, otsatira ake anafalitsa Chikristu kumayiko ena. Cha m’ma 60 ndi 61 C.E., ‘uthenga wabwino unalalikidwa cholengedwa chonse cha pansi pa thambo.’ (Akol. 1:6, 23) Kuyambira pamenepo, uthenga wabwino umenewuwafikadi ku “malekezero ake a dziko.”

[Bokosi patsamba 32]

ANACHOKERA KU . . .

Ayuda ndi oloŵa Chiyuda omwe anamva uthenga wabwino pa Pentekoste 33 C.E. anachokera ku Aparti, Mediya, Elamu, Mesopotamiya, Yudeya, Kapadokiya, Ponto, Asiya, Frugiya, Pamfuliya, Igupto, Libiya, Roma, Kurene, ndi Arabiya. Ambiri anabatizidwa. Kodi mukuganiza kuti anakachita chiyani atabwerera kwawo?

[Bokosi patsamba 33]

MIPINGO ISANU NDI IŴIRI

Yesu anatumiza uthenga ku mipingo isanu ndi iŵiri ku Asiya Mina. Onani malo amene mipingoyo inali: kunyanja ku Efeso ndi Smurna; kumtunda ku Pergamo, Filadelfeya, ndi Laodikaya; Tiyatira umene unali m’mphepete mwa mtsinje; ndi Sarde umene unali panjira yamalonda. Zotsalira za mizinda imeneyi zimene zafukulidwa zimasonyeza kuti Baibulo limanena za malo enieni.

[Mapu patsamba 32]

(Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)

Spread of Christianity

Madera Amene Uthenga Wabwino Unafika Msanga

B1 ILURIKO

B1 ITALIYA

B1 Roma

C1 MAKEDONIYA

C2 GIRISI

C2 Atene

C2 KRETE

C3 Kurene

C3 LIBIYA

D1 BITUNIYA

D2 GALATIYA

D2 ASIYA

D2 FRUGIYA

D2 PAMFULIYA

D2 KUPRO

D3 IGUPTO

D4 ITIOPIYA

E1 PONTO

E2 KAPADOKIYA

E2 KILIKIYA

E2 MESOPOTAMIYA

E2 SURIYA

E3 SAMARIYA

E3 Yerusalemu

E3 YUDEYA

F2 MEDIYA

F3 Babulo

F3 ELAMU

F4 ARABIYA

G2 PARTHIA

[Nyanja]

C2 Nyanja ya Mediterranean

D1 Nyanja Yakuda

E4 Nyanja Yofiira

F3 Nyanja Ya Perisiya

[Mapu patsamba 32, 33]

(Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)

Maulendo a Paulo

Ulendo Woyamba Waumishonale (Mac. 13:1–14:28)

H3 Antiokeya (wa Suriya)

H3 Selukeya

G4 KUPRO

G3 Salami

G4 Pafo

G3 PAMFULIYA

F3 Perge

F3 PISIDIYA

F2 Antiokeya (wa Pisidiya)

G2 Ikoniyo

G2 LUKAONIYA

G2 Lustra

G3 Derbe

G2 Lustra

G2 Ikoniyo

F2 Antiokeya (wa Pisidiya)

F3 PISIDIYA

G3 PAMFULIYA

F3 Perge

F3 Ataliya

H3 Antiokeya (wa Suriya)

Ulendo Wachiŵiri Waumishonale (Mac. 15:36–18:22)

H3 Antiokeya (wa Suriya)

H3 SURIYA

H3 KILIKIYA

H3 Tariso

G3 Derbe

G2 Lystra

G2 Ikoniyo

F2 Antiokeya (wa Pisidiya)

F2 FRUGIYA

G2 GALATIYA

E2 MUSIYA

E2 Trowa

E1 SAMATRAKE

D1 Neapoli

D1 Filipi

C1 MAKEDONIYA

D1 Amfipoli

D1 Tesalonika

D1 Bereya

C2 GIRISI

D2 Atene

D2 Korinto

D3 AKAYA

E2 Efeso

G4 Kaisareya

H5 Yerusalemu

H3 Antiokeya (wa Suriya)

Ulendo Wachitatu Waumishonale (Mac. 18:22–21:19)

H3 SURIYA

H3 Antiokeya (wa Suriya)

G2 GALATIYA

F2 FRUGIYA

H3 KILIKIYA

H3 Tariso

G3 Derbe

G2 Lystra

G2 Ikoniya

F2 Antiokeya (wa Pisidiya)

E2 Efeso

E2 ASIYA

E2 Troas

D1 Filipi

C1 MAKEDONIYA

D1 Amfipoli

D1 Tesalonika

D1 Bereya

C2 GIRISI

D2 Atene

D2 Korinto

D1 Bereya

D1 Tesalonika

D1 Amfipoli

D1 Filipi

E2 Troas

E2 Aso

E2 Mitilene

E2 KIYO

E2 SAMO

E3 Mileto

E3 Ko

E3 RODE

F3 Patara

H4 Turo

H4 Ptolemayi

G4 Kaisareya

H5 Yerusalemu

Ulendo wa ku Roma (Mac. 23:11–28:31)

H5 Yerusalemu

G4 Kaisareya

H4 Sidoni

F3 Mura

F3 LUKIYA

E3 Knido

D3 KRETE

D4 KAUDA

A3 MELITA

A3 SICILY

A3 Surakusa

A1 ITALIYA

B2 Regio

A1 Potiyolo

A1 Roma

Njira Zazikulu (Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)

[Mipingo isanu ndi iŵiri]

E2 Pergamo

E2 Tiyatira

E2 Sarde

E2 Smurna

E2 Efeso

F2 Filadelfeya

F2 Laodikaya

[Malo Ena]

E3 PATMO

F2 Kolose

F5 Alesandriya

F5 IGUPTO

G1 BITUNIYA

G5 Yopa

G5 Luda

G5 Gaza

H1 PONTO

H2 KAPADOKIYA

H4 Damasiko

H4 Pella

[Nyanja]

Nyanja ya Mediterranean

[Chithunzi patsamba 33]

Bwalo la ku Mileto, mzinda umene Paulo anakumanako ndi akulu ochokera ku Efeso

[Chithunzi patsamba 33]

Guwa la nsembe la Zeu ku Pergamo. Akristu a mu mzinda umenewu ankakhala kumene ‘kunali mpando wachifumu wa Satana’—Chiv. 2:13

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena