Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 12/97 tsamba 1
  • Amakusoŵanitu!

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Amakusoŵanitu!
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Mumathandiza Kuti Misonkhano Yachikhristu Ikhale Yolimbikitsa?
    Nsanja ya Olonda—2010
  • N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kusonkhana?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
  • Ndandanda ya Banja ya Misonkhano ya Mpingo
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kusonkhana?
    Nsanja ya Olonda—2007
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
km 12/97 tsamba 1

Amakusoŵanitu!

1 Nthaŵi ndi nthaŵi, tingamalephere kufika pamsonkhano wampingo umodzi kapena ingapo, tikumaganiza kuti ‘palibe yemwe adzandisoŵa; sangaone nkomwe kuti ineyo palibepo.’ Si zoona zimenezo! Monga chiwalo cha thupi lathuli, aliyense amachita mbali yofunika kuti mpingo uziyenda bwino. (1 Akor. 12:12) Tikamasoŵeka pamsonkhano wa mlungu ndi mlungu timadodometsa mtendere wauzimu wa amene amapezekapo. Ngati inu palibepo, dziŵani kuti—amakusoŵanitu!

2 Mbali Yofunika Imene Mumachita: Paulo analakalaka kusonkhana ndi abale ake. Aroma 1:11, 12, amafotokoza chifukwa chake: “Kuti ndikagaŵire kwa inu mtulo wina wauzimu, . . . kuti ine ndikatonthozedwe pamodzi ndi inu, mwa chikhulupiriro cha ife tonse aŵiri, chanu ndi changa.” Momwemonso, mwa mayankho athu, nkhani zimene timakamba pamsonkhano, ndiponso mwa kungopezekapo, timalimbikitsa ena kuyendabe mokhulupirika.—1 Ates. 5:11.

3 Kodi simumayembekezera mwachidwi kukaona ena pamisonkhano yampingo? Mumatchera khutu iwo akamayankha ndipo mumayamikira mmene amasonyezera chikhulupiriro chawo. Mphatso zawo zauzimu zimathandizira kukulimbikitsani. Ngati iwo sanapezekepo pamsonkhanopo, mumamva kuti pasoŵeka kanthu kena kofunika. Abale anu ndi alongo anu amamvanso choncho ngati inuyo simunapezekepo.

4 Mbali Yofunika Imene Misonkhano Imachita: Panthaŵi ina, Nsanja ya Olonda inafotokoza mmene misonkhano ilili yofunika pakutithandiza kukhalabe amoyo mwauzimu. Inati: “M’dziko lino lodzaza ndi mikangano ndi chisembwere, mpingo Wachikristu ulidi pothaŵirapo pauzimu penipeni . . . , uli phanga la mtendere ndi chikondi. Chotero, khalani wofika pamisonkhano yake yonse wokhazikika.” (w93-CN 8/15 11) Tsiku lililonse, timakumana ndi zothetsa nzeru zomwe zimatilemetsa mwauzimu. Ngati sitisamala, tingamire m’nkhaŵa zathu moti tingaiŵale zinthu zofunika zauzimu. Tonsefe timadalira ena kuti atilimbikitse kuti tikhalebe ogwirizana ndi achangu mu utumiki wa Mulungu.—Aheb. 10:24, 25.

5 Kupezeka pamisonkhano nkofunika. Matenda kapena zina zogwa mwadzidzidzi zingatilepheretse nthaŵi zina. Komabe, tiyeni tizitsimikiza nthaŵi zonse kuti azitiŵerengera pamasonkhano a anthu otamanda Yehova pamodzi!—Sal. 26:12.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena