Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 2/00 tsamba 7
  • Bokosi la Mafunso

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Bokosi la Mafunso
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
  • Nkhani Yofanana
  • Kuyesetsa Kuti Anthu Mumpingo Apitirize Kukhala Amtendere Komanso Oyera
    Gulu Lochita Chifuniro cha Mulungu
  • Landirani Chilango cha Yehova Nthawi Zonse
    Nsanja ya Olonda—2006
  • Tsanzirani Chifundo cha Yehova
    Nsanja ya Olonda—1998
  • Kodi Mpingo Ungatsanzire Bwanji Maganizo a Yehova pa Nkhani ya Anthu Ochimwa?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2024
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
km 2/00 tsamba 7

Bokosi la Mafunso

◼ Kodi n’koyenera kuwombera m’manja chilengezo cha kubwezeretsedwa?

Chifukwa cha kukoma mtima kwake kwachikondi, Yehova Mulungu wapereka njira ya Malemba yakuti ochita zoipa olapa apezenso chiyanjo chake ndi kubwezeretsedwa mu mpingo wachikristu. (Sal. 51:12, 17) Zimenezi zikachitika, timalimbikitsidwa kuwatsimikizira chikondi chathu anthu olapa moona mtima ameneŵa.—2 Akor. 2:6-8.

Ngakhale kuti timasangalala kwambiri pamene wachibale wathu kapena mnzathu wabwezeretsedwa, tiyenera kukhala chete pamene akulengeza mu mpingo za kubwezeretsedwa kwake. Nsanja ya Olonda ya October 1, 1998 patsamba 17 inanena nkhaniyi motere: “Komabe, tikumbukire kuti ambiri mumpingo sakudziŵa zimene zinachotsetsa munthuyo kapena zimene zachititsa kuti abwezeretsedwe. Ndiponso, pangakhale ena amene anakhudzidwa mtima kwambiri kapena kukhumudwa mwina kwanthaŵi yaitali chifukwa cha tchimo la munthu wolapayo. Chifukwa chozindikira zinthu ngati zimenezo, tidzapeŵa mawu akuti tam’landira polengeza kubwezeretsedwa kwake. Tidzasiyira nkhani imeneyo kwa munthu aliyense payekha kuti adzilankhulire yekha pokambirana naye wobwezeretsedwayo.”

Ngakhale timakondwa kwambiri kuona kuti wina wabwerera m’choonadi, kuwombera m’manja panthaŵi imene iye akubwezeretsedwa n’kosayenera.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena