Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb25 March tsamba 14-15
  • April 28–May 4

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • April 28–May 4
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
mwb25 March tsamba 14-15

APRIL 28–MAY 4

MIYAMBO 11

Nyimbo Na. 90 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Musamalankhule

(10 min.)

Musamalankhule chilichonse chimene chikhoza kuwononga ‘mnzanu’ (Miy 11:9; w02 5/15 26 ¶4)

Musamalankhule zinthu zimene zingayambanitse anthu, kapena zimene zikunena zoipa za munthu wina, komanso musamangokhalira kudandaula (Miy 11:11; w02 5/15 27 ¶3-4)

Musamalankhule nkhani zachinsinsi za ena (Miy 11:12, 13; w02 5/15 27 ¶6)

Abale awiri akulankhulana pa Nyumba ya Ufumu. M’bale wina akulankhula zoipa zokhudza m’bale wina amene akudutsa chapafupi.

FUNSO LOFUNIKA KULIGANIZIRA: Kodi mawu a Yesu opezeka pa Luka 6:45 angatithandize bwanji kuti tizilankhula bwino?

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Miy 11:17—Kodi ifeyo zinthu zimatiyendera bwanji tikakhala okoma mtima? (g20.1 11, bokosi)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Miy 11:1-20 (th phunziro 5)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(4 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Pezani mwayi woti mumuuze zimene munaphunzira pamisonkhano yampingo yaposachedwapa. (lmd phunziro 2 mfundo 4)

5. Ulendo Wobwereza

(4 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Gwiritsani ntchito vidiyo yopezeka pa Zinthu Zophunzitsira. (lmd phunziro 8 mfundo 3)

6. Kuphunzitsa Anthu

(4 min.) KULALIKIRA M’MALO OPEZEKA ANTHU AMBIRI. M’pempheni kuti muziphunzira naye Baibulo ndipo musonyezeni mmene phunziroli limachitikira. (lmd phunziro 10 mfundo 3)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 157

7. Musalole Kuti Lilime Lanu Lizisokoneza Mtendere

(15 min.) Nkhani yokambirana.

Chifukwa choti ndife opanda ungwiro, nthawi zina timalankhula zolakwika. (Yak 3:8) Komabe, kuganizira mavuto amene amabwera chifukwa cholankhula zolakwika, kumatithandiza kupewa kulankhula zinthu zimene pamapeto pake tinganong’oneze nazo bondo. Tiyeni tione zinthu zina zofunika kupewa zomwe tikalankhula zingasokoneze mtendere mumpingo.

  • Kudzitamandira. Munthu akamadzitamandira amadzionetsa kuti ndi wapamwamba kwambiri zomwe zingayambitse mpikisano komanso nsanje.—Miy 27:2

  • Kusalankhula zoona. Kusalankhula zoona sikutanthauza kunena bodza kokha komanso ngakhale kunena zinthu zomwe zingasocheretse ena. Kusalankhula zoona ngakhale pa nkhani yaing’ono kungachititsenso kuti ena asiye kukukhulupirirani komanso kungawononge mbiri yanu.—Mla 10:1

  • Miseche. Munthu wamiseche amakamba nkhani zabodza za ena kapena amaulula zinsinsi za ena. (1Ti 5:13) Zimenezi zingayambitse mikangano komanso zingachititse kuti anthu asamagwirizane

  • Mawu aukali. Munthu amalankhula mawu aukali akalephera kudziletsa pamene wakwiya ndi zimene winawake wachita kapena kulankhula. (Aef 4:26) Mawu aukali amapweteka.—Miy 29:22

Zithunzi za muvidiyo yakuti “Muzipewa Zinthu Zomwe Zingasokoneze Mtendere—Kachigawo Kake.” 1. Emily ndi Cecelia akhala moyang’anizana pa lesitilanti. Cecelia akuona pafoni yake zimene Haley waika pamalo ochezera a pa intaneti. 2. Haley akumulankhula Cecelia mopsa mtima pa malo oimika magalimoto ku Nyumba ya Ufumu

Onerani VIDIYO yakuti Muzipewa Zinthu Zomwe Zingasokoneze Mtendere—Kachigawo Kake. Kenako funsani funso lotsatirali:

  • Kodi mwaphunzira chiyani pa mmene mawu athu angasokonezere mosavuta mtendere mumpingo?

Kuti muone mmene ena anabwezeretsera mtendere, onerani vidiyo yakuti Muzifunafuna “Mtendere ndi Kuusunga.”

8. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) bt mutu 25 ¶14-21

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Yatsopano ya Msonkhano wa 2025 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena