Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb25 May tsamba 12-13
  • June 16-22

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • June 16-22
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
mwb25 May tsamba 12-13

JUNE 16-22

MIYAMBO 18

Nyimbo Na. 90 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Muzilankhula Mawu Olimbikitsa kwa Anthu Amene Akudwala

(10 min.)

Muzilola kuti nzeru yochokera kwa Mulungu izikuthandizani kudziwa zimene mungalankhule (Miy 18:4; w22.10 22 ¶17)

Muziyesetsa kumvetsa zimene munthuyo akukumana nazo (Miy 18:13; mrt nkhani na. 19 bokosi)

Muzikhala bwenzi lothandiza komanso loleza mtima (Miy 18:24; wp23.1 14 ¶3–15 ¶1)

Mwamuna akumvetsera mwachifundo pamene mkazi wake akumufotokozera mmene akumvera.

DZIFUNSENI KUTI, ‘Kodi ndingathandize bwanji mkazi kapena mwamuna wanga ngati akudwala matenda enaake kapena ngati ali ndi vuto linalake la mu ubongo?’

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Miy 18:18—N’chifukwa chiyani anthu a m’nthawi za m’Baibulo ankachita maere? (it-2 271-272)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Miy 18:1-17 (th phunziro 11)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(1 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Munthuyo amalankhula chilankhulo china. (lmd phunziro 2 mfundo 5)

5. Ulendo Wobwereza

(3 min.) KULALIKIRA M’MALO OPEZEKA ANTHU AMBIRI. Mwininyumba wakuuzani kuti ali ndi nthawi yochepa. (lmd phunziro 7 mfundo 4)

6. Ulendo Wobwereza

(3 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. M’phunzitseni mfundo yofunika ya choonadi yokhudza Ufumu wa Mulungu. (lmd phunziro 9 mfundo 5)

7. Kufotokoza Zimene Mumakhulupirira

(4 min.) Chitsanzo. ijwfq nkhani na. 29—Mutu: Kodi Mumakhulupirira Kuti Dzikoli Linalengedwa M’masiku 6 Enieni? (lmd phunziro 5 mfundo 5)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 144

8. Kuthandiza Anthu Amene Mumawakonda Kukhala Anzake a Yehova Popanda Kulankhula

(15 min.) Nkhani yokambirana.

Ambirife tikudziwa munthu wina amene panopa satumikira Yehova. Mwina mwamuna kapena mkazi wathu, mwana wathu kapena mnzathu amene tinkamukonda koma anasiya kutumikira Yehova. Kodi munazindikira kuti nthawi zina mumachita zinthu mokakamiza mwinanso mwamwano kumene poyesa kumuthandiza kuti ayambirenso kutumikira Yehova? N’zoona kuti tingakhale ndi zolinga zabwino, koma mawu athu akhoza kuwononga zinthu. (Miy 12:18) Ndiye kodi njira yabwino yomuthandizira ingakhale iti?

Lemba la 1 Petulo 3:1 limanena kuti mwamuna wosakhulupirira akhoza kukopeka “osati ndi mawu” okha. Ngakhale mwamuna wa mlongo wa Chikhristu atamakana kukambirana naye mfundo za choonadi cha m’Baibulo, akhozabe kumuthandiza kudziwa Yehova. Zochita za mlongoyo zomwe zimatsogoleredwa ndi makhalidwe abwino monga chikondi, ubwino ndi nzeru zikhoza kufewetsa mtima wa mwamuna wakeyo. (Miy 16:23) Kuchita zinthu mokoma mtima ndi anthu amene timawakonda koma satumikira Yehova kukhoza kukhala ndi zotsatira zabwino.

Onerani VIDIYO yakuti Anthu Omwe Apambana pa Nkhondo Yachikhulupiriro—Amene Ali pa Banja Ndi Munthu Wosakhulupirira. Kenako funsani mafunso otsatirawa:

    Chithunzi cha muvidiyo yakuti “Anthu Omwe Apambana pa Nkhondo Yachikhulupiriro—⁠Amene Ali pa Banja Ndi Munthu Wosakhulupirira.” Mlongo Hideko Sasaki.
  • Kodi mwaphunzira chiyani kuchokera pa zimene zinachitikira Mlongo Sasaki?

  • Chithunzi cha muvidiyo yakuti “Anthu Omwe Apambana pa Nkhondo Yachikhulupiriro—⁠Amene Ali pa Banja Ndi Munthu Wosakhulupirira.” Mlongo Noriko Ito.
  • Kodi mwaphunzira chiyani kuchokera pa zimene zinachitikira Mlongo Ito?

  • Chithunzi cha muvidiyo yakuti “Anthu Omwe Apambana pa Nkhondo Yachikhulupiriro—⁠Amene Ali pa Banja Ndi Munthu Wosakhulupirira.” Mlongo Tomoe Okada.
  • Kodi mwaphunzira chiyani kuchokera pa zimene zinachitikira Mlongo Okada?

9. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) bt mutu 27 ¶23-26, bokosi patsamba 214 ndi 217

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 60 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena