Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb25 November tsamba 2-3
  • November 3-9

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • November 3-9
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
mwb25 November tsamba 2-3

NOVEMBER 3-9

NYIMBO YA SOLOMO 1-2

Nyimbo Na. 132 ndi Pempher | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Nkhani ya Chikondi Chenicheni

(10 min.)

[Onerani VIDIYO yakuti Mfundo Zothandiza Kumvetsa Buku la Nyimbo ya Solomo.]

Solomo anayamikira kwambiri Msulami ndipo anamulonjeza kuti amupatsa zinthu zamtengo wapatali (Nym 1:​9-11)

Chifukwa chakuti Msulami ankakonda kwambiri m’busa, iye anakhalabe wokhulupirika kwa m’busayo (Nym 2:​16, 17; w15 1/15 30 ¶9-​10)

Solomo akuitana Msulami kuti apite kutenti yake, koma Msulamiyo akukana ndipo wayang’ana kumbali komanso wapinda manja ake. Antchito atatu a Solomo aima patsogolo pa tenti ndipo wina wanyamula thaulo, wina wanyamula beseni pamene winayo wanyamula jagi.

ZIMENE ZINGAKUTHANDIZENI: Kuti mudziwe amene akulankhula mukamawerenga buku la Nyimbo ya Solomo, muzigwiritsa ntchito gawo la mu Baibulo la Dziko Latsopano lakuti “Zimene Zili M’bukuli.”

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Nym 2:7-N’chifukwa chiyani Msulami ndi chitsanzo chabwino kwa Akhristu omwe sali pabanja? (w15 1/15 31 ¶11)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Nym 2:1-17 (th phunziro 12)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(3 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Kambiranani mfundo imodzi ya choonadi mu zakumapeto A, m’kabuku kakuti Muzikonda Anthu. (lmd phunziro 1 mfundo 3)

5. Ulendo Wobwereza

(4 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Kambiranani mfundo imodzi ya choonadi mu zakumapeto A, m’kabuku kakuti Muzikonda Anthu. (lmd phunziro 9 mfundo 3)

6. Kuphunzitsa Anthu

(5 min.) lff phunziro 18 mawu oyamba komanso mfundo 1-3. (th phunziro 8)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 46

7. “Munthu Wowolowa Manja Adzadalitsidwa”

(15 min.) Nkhani yokambirana. Ikambidwe ndi mkulu.

Tikamagwiritsa ntchito nthawi, mphamvu komanso zinthu zathu pothandiza ena, timadalitsidwa kwambiri. N’zoona kuti munthu akalandira mphatso amaiona kuti ndi dalitso, koma amene waperekayo nayenso amadalitsidwa. (Miy 22:9) Munthu amene amachita zimenezi amakhala wosangalala chifukwa chakuti akutsanzira Yehova ndipo Yehovayo amasangalala naye.​—Miy 19:17; Yak 1:​17.

Kamtsikana kukuponya ndalama mubokosi la zopereka.
Bambo akutchera foni yake kuti izitumiza zopereka mwezi uliwonse.

Onerani VIDIYO yakuti Kuwolowa Manja Kumatithandiza Kukhala Osangalala. Kenako funsani mafunso awa:

  •  Kodi anthu a muvidiyoyi anasangalala bwanji chifukwa cha kuwolowa manja kwa abale ndi alongo padziko lonse lapansi?

  •  Kodi anthuwa anamva bwanji chifukwa chakuti nawonso anathandiza ena mowolowa manja?

Dziwani Zambiri Pawebusaiti Yathu

Chizindikiro cha “Donations” chosonyeza dzanja litanyamula ndalama ya chitsulo.

Kodi mungapereke bwanji ndalama zothandizira ntchito ya Mboni za Yehova? Dinani pamene alemba kuti “Donations” m’munsi mwa tsamba loyamba la JW Library®. M’mayiko ambiri, patsambali mungapezepo tabu ya Mafunso Ofunsidwa Kawirikawiri yomwe ingakupititseni ku failo ya mutu wakuti Zopereka Zopita ku Gulu la Mboni za Yehova—Mafunso Ofunsidwa Kawirikawiri.

8. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) lfb mutu 32-33

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 137 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena