Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb25 November tsamba 4-5
  • November 10-16

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • November 10-16
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
mwb25 November tsamba 4-5

NOVEMBER 10-16

NYIMBO YA SOLOMO 3-5

Nyimbo Na. 31 ndi Pemphero Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Kukongola kwa Mumtima Ndi Kofunika

(10 min.)

Kukongola kwa mumtima kwa Msulami kunkaonekera mu zolankhula zake (Nym 4:​3, 11; w15 1/15 30 ¶8)

Makhalidwe ake abwino, ankayerekezeredwa ndi munda wa maluwa wokongola kwambiri (Nym 4:​12; w00 11/1 11 ¶17)

Aliyense akhoza kukhala wokongola mumtima, zomwe ndi zofunika kwambiri kuposa kukongola kwa kunja (g05 1/8 25 ¶2-5)

Zithunzi: 1. Mlongo akulimbikitsa mlongo wachitsikana yemwe ali ndi nkhawa. 2. M’bale wachinyamata akuthandiza mosangalala m’bale wachikulire pamene ali limodzi muutumiki.

DZIFUNSENI KUTI, ‘Kodi ndi makhalidwe auzimu ati amene ndimachita nawo chidwi mwa anthu ena?’

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Nym 3:5—N’chifukwa chiyani “ana aakazi a ku Yerusalemu” analumbiritsidwa “pali insa ndiponso pali mphoyo zakutchire”? (w06 11/15 18 ¶4)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Nym 4:1-16 (th phunziro 2)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(3 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. M’pempheni mwachindunji kuti muziphunzira naye Baibulo. (lmd phunziro 6 mfundo 4)

5. Ulendo Woyamba

(4 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Muonetseni mmene angapezere zinthu m’chilankhulo chake pa jw.org. (lmd phunziro 4 mfundo 3)

6. Nkhani

(5 min.) ijwbq nkhani Na. 131—Mutu: Kodi Baibulo Limati Chiyani pa Nkhani ya Kudziphoda Komanso Kuvala Zodzikongoletsera? (th phunziro 1)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 36

7.Kwatirani mwa Ambuye (Ge 28:2)

(8 min.)

Onerani VIDIYO.

8. Kodi Mudzakhala Mwamuna Kapena Mkazi Wabwino kwa Munthu Amene Mudzakwatirane Naye?

(7 min.) Nkhani yokambirana.

Kodi mukufunafuna mkazi kapena mwamuna woti mukwatirane naye? Kodi inuyo muli ndi makhalidwe auzimu omwe Akhristu ena amene akufuna wokwatirana naye angasangalale nawo? Ngakhale kuti poyamba munthu akhoza kumachita zinthu ngati wauzimu, koma m’kupita kwa nthawi makhalidwe ake enieni amaonekera.

Mlongo akupereka mpando umene anakhala m’basi kwa mayi wachikulire.
M’bale akupereka kapepala kwa mnzake wa kuntchito pamene akuweruka ku ntchito yawo ya zomangamanga.
Abale awiri ndi alongo awiri akulalikira limodzi. M’bale mmodzi akulozera alongowo kumene akufunika akalalikire.

M’munsimu, lembani vesi la m’Baibulo logwirizana ndi makhalidwe amene munthu wauzimu amasonyeza.

  • Kukonda Yehova ndi kumukhulupirira

  • Kukhala mutu wabanja wabwino, kapena mkazi amene angamalemekeze mwamuna wake

  • Kusadzikonda ndi kukhala ndi chikondi chovutikira ena

  • Kuganiza bwino, kudziwa malire komanso kulolera

  • Khama ndiponso kulimbikira ntchito

9. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) lfb mutu 34-35

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 44 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena