Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • le tsamba 11-13
  • Kodi Mulungu Adzawononganso Anthu Oipa?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mulungu Adzawononganso Anthu Oipa?
  • Sangalalani Ndi Moyo pa Dziko Lapansi Kosatha!
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Tiyenera Kuchita Chiyani Kuti Tikondweretse Mulungu?
    Mverani Mulungu Kuti Mudzapeze Moyo Wosatha
  • Kodi N’chiyani Chimene Muyenera Kuchita?
    Sangalalani Ndi Moyo pa Dziko Lapansi Kosatha!
  • Chigawo 13
    Mverani Mulungu
  • Kodi Tiyenera Kugwiritsa Ntchito Mafano Polambira Mulungu?
    Galamukani!—2008
Onani Zambiri
Sangalalani Ndi Moyo pa Dziko Lapansi Kosatha!
le tsamba 11-13

Kodi Mulungu Adzawononganso Anthu Oipa?

22 Anthu lerolino alinso oipa kwambiri. Kodi ndi zinthu zoipa zotani zimene zikuchitidwa?

23 Ena amapha anthu ena. Mulungu amanena kuti simuyenera kuchita izi.—Eksodo 20:13; 1 Yohane 3:11, 12

24 Ena amaba. Mulungu amanena kuti simuyenera kuba.—Eksodo 20:15; Aefeso 4:28

25 Anthu ena amakwatira akazi ambiri. Ena amakhala ndi akazi aŵiri kapena oposerapo m’nyumba zosiyanasiyana. Enanso mwamuna ndi mkazi amakhalira limodzi popanda kukwatirana. Zonsezi ndi zosemphana ndi zimene Baibulo limanena.—Mateyu 19:4-6; 1 Akorinto 7:1-4; 1 Timoteo 3:1, 2

26 Kodi mukukumbukira kuti Mulungu anapatsa Adamu mkazi mmodzi yekha?—Genesis 2:22, 24

27 Ena amalambira mafano. Mulungu amanena kuti musagwiritsire ntchito mafano kapena zifanizo m’kulambira.—Eksodo 20:4, 5; Yesaya 44:9-17; 1 Yohane 5:21

28 Yehova adzawononga oipa amene sakasintha.—Salmo 37:9, 10; Luka 13:5; 1 Akorinto 6:9, 10

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena