Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w10 11/1 tsamba 3
  • Kodi Munthu Angakhaledi Wokhutira ndi Zimene ali Nazo?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Munthu Angakhaledi Wokhutira ndi Zimene ali Nazo?
  • Nsanja ya Olonda—2010
  • Nkhani Yofanana
  • Tsatirani Mfundo za M’Baibulo Kuti Mupeze Chimwemwe
    Nsanja ya Olonda—2006
  • Kodi Ndalama Tingazione Motani M’njira Yoyenera?
    Nsanja ya Olonda—2001
  • Muzisankha Mwanzeru Anthu Ocheza Nawo
    Nsanja ya Olonda—2010
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2010
w10 11/1 tsamba 3

Kodi Munthu Angakhaledi Wokhutira ndi Zimene ali Nazo?

“Osauka amalemera chifukwa chokhutira ndi zimene ali nazo koma olemera amasauka chifukwa chosakhutira ndi zimene ali nazo.”​—Benjamin Franklin.

MOGWIRIZANA ndi mawu amenewa, anthu ambiri azindikira kuti sichinthu chapafupi kuti munthu azikhutira ndi zimene ali nazo. N’chifukwa chake n’zosadabwitsa kuti anthu ambiri masiku ano sakhutira ndi zimene ali nazo. Izi zili choncho chifukwa anthu m’dzikoli amakonda kusirira za anthu ena ndipo amalimbikitsa mtima wokonda chuma ndiponso kutchuka. Kodi n’kutheka kuti zinthu zotsatirazi zakuchitikiraninso inuyo?

• Otsatsa malonda amachititsa anthu kuganiza kuti angakhale okhutira pa moyo wawo atangogula chinthu chimodzi kuwonjezera pa zimene ali nazo kale.

• Anthu ambiri ku ntchito kapena ku sukulu amalimbikitsa anzawo kuona kuti angakhale ofunika ngati atamachita zimene anthu ena akuchita.

• Anthu ambiri sayamika wina akawachitira zabwino.

• Anthu amafuna kuti anzawo azisilira zinthu iwo ali nazo.

• Anthu ambiri sapeza mayankho a mafunso ofunika amene ali nawo.

Ndiye tikaganizira mavuto onsewa, kodi n’zothekadi kukhala okhutira ndi zinthu zimene tili nazo? Mtumwi Paulo ananena za “chinsinsi chakukhala wokhutitsidwa.” Nthawi zina ankakhala ndi zinthu zambiri pomwe nthawi zina ankakhala ndi zochepa. Anzake ankamusilira pomwe anthu ena ankamunyoza. Komabe iye ananena kuti: “Ndaphunzira chinsinsi chakukhala wokhutitsidwa mwa njira ina iliyonse.”​—Mawu tapendeketsa tokha; Afilipi 4:11, 12, Chipangano Chatsopano Mu Chichewa Cha Lero.

Anthu amene sanayesepo kukhala moyo wokhutira ndi zimene ali nazo amaganiza kuti n’zosatheka kukhala moyo umenewu. Koma mtumwi Paulo ananena kuti anthu oterewa akhoza kuphunzira kukhala wokhutira. Tsopano tiyeni tione mfundo zisanu zopezeka m’Baibulo, lomwe ndi Mawu a Mulungu, zimene zingatithandize kukhala okhutira ndi zimene tili nazo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena