Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w13 11/15 tsamba 8-9
  • Kodi Tingathandize Bwanji Anthu Ena?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Tingathandize Bwanji Anthu Ena?
  • Nsanja ya Olonda—2013
  • Nkhani Yofanana
  • Zochuluka Zimene Anali Nazo Zinathandiza Anthu Osowa
    Nsanja ya Olonda—2012
  • “Ntchitoyi Ndi Yaikulu”
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
  • Tiziyamikira Zimene Yehova Amatipatsa
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Yehova Amadalitsa Anthu Opereka ndi Mtima Wonse
    Nsanja ya Olonda—2014
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2013
w13 11/15 tsamba 8-9

Kodi Tingathandize Bwanji Anthu Ena?

M’BALE wina dzina lake François amene ndi mkulu kudziko lina anati: “Anthu amene anakana zotsatira za chisankho anayambitsa chipolowe ndipo abale ndi alongo ambirimbiri anathawa m’nyumba zawo. Chakudya ndi mankhwala zinayamba kusowa ndipo zimene zinkapezeka zinali zodula kwambiri. Mabanki anatsekedwa ndipo makina otapira ndalama anasiya kugwira ntchito.”

Mwamsanga abale ochokera ku ofesi ya nthambi anayamba kupereka ndalama ndiponso zinthu zina zofunika kwa abale ndi alongo amene anathawira ku Nyumba za Ufumu. Magulu amene ankalimbanawo anatseka misewu. Koma ankalola magalimoto ochokera kunthambi kudutsa chifukwa ankadziwa kuti a Mboni salowerera ndale.

François anati: “Pamene tinkapita ku Nyumba ya Ufumu ina, anthu anayamba kuwombera galimoto yathu. Zipolopolo zinkadutsa pafupi kwambiri koma mwamwayi sanatiwombere. Kenako tinaona msilikali wonyamula chida akutithamangira. Nthawi yomweyo tinatembenuza galimoto n’kubwerera kunthambi. Tinathokoza Yehova kuti tinapulumuka. Tsiku lotsatira abale ndi alongo 130 amene anali m’Nyumba ya Ufumu imeneyo anathawa n’kukabisala kwina. Ena anabwera ku ofesi ya nthambi ndipo tinawathandiza komanso kuwalimbikitsa mpaka pamene mavutowo anatha.”

François ananenanso kuti: “Abale ambiri anatumiza makalata oyamikira kwambiri zimene abale awo anachita powathandiza. Kuona abale ochokera kwina akuwathandiza kunawalimbikitsa kukhulupirira kwambiri Yehova.”

Pakagwa mavuto, sitimangouza abale ndi alongo ovutika kuti “mupeze zovala ndi zakudya za tsiku lililonse.” (Yak. 2:15, 16) Koma timayesetsa kuwathandiza kupeza zinthu ngati zimenezi. Umu ndi mmene zinalili m’nthawi ya atumwi. Ophunzira atamva kuti kudzakhala njala, “anatsimikiza mtima kutumiza thandizo lililonse limene akanatha kwa abale okhala ku Yudeya.”—Mac. 11:28-30.

Atumiki a Yehovafe timafunitsitsa kuthandiza anthu ovutika. Koma anthu amakhalanso ndi zosowa zauzimu. (Mat. 5:3) Pofuna kuthandiza anthu kudziwa ndiponso kupeza zosowa zawo zauzimu, Yesu analamula otsatira ake kuti aziphunzitsa anthu. (Mat. 28:19, 20) Tonse timayesetsa kugwiritsa ntchito nthawi yathu, mphamvu zathu ndiponso chuma chathu kuti tigwire ntchito imeneyi. Gulu lathu limagwiritsa ntchito ndalama zina pothandiza anthu ovutika. Koma zopereka zambiri zimagwiritsidwa ntchito pothandiza kuti tilalikire uthenga wabwino. Pochita zimenezi timasonyeza kuti timakonda Mulungu ndiponso anzathu.—Mat. 22:37-39.

Anthu amene amapereka ndalama zothandiza pa ntchito yapadziko lonse ya Mboni za Yehova ayenera kudziwa kuti ndalamazo zikugwiritsidwa ntchito moyenera. Kodi inuyo mungathandize abale anu amene akuvutika? Kodi mumafunitsitsa kuthandiza pa ntchito yolalikira? Ngati zili choncho, ‘musalephere kuchitira zabwino anthu amene akufunikira zabwinozo, pamene dzanja lanu lingathe kuchita zimenezo.’—Miy. 3:27.

ZIMENE ENA AMAPEREKA PA NTCHITO YAPADZIKO LONSE

Mofanana ndi nthawi ya Paulo, Akhristu ambiri masiku ano amapanga bajeti kapena kuika kandalama “kenakake pambali” kuti akaponye m’mabokosi a zopereka za “Ntchito Yapadziko Lonse.” (1 Akor. 16:2) Mwezi uliwonse mipingo imatumiza zopereka zimenezi ku ofesi ya Mboni za Yehova m’dziko lawo. N’zothekanso kutumiza nokha zopereka zanu ku maofesi ngati amenewa. Mungafunse ku ofesi ya nthambi m’dziko lanu kuti mudziwe mmene mungachitire zimenezi. Adiresi ya ofesi ya nthambi iliyonse imapezeka pa webusaiti ya www.jw.org. Mungapereke zopereka zanu m’njira izi:

  • ZOPEREKA MWACHINDUNJI

    • Mukhoza kupereka ndalama, zinthu ngati ndolo, mphete, zibangiri ndiponso zinthu zina zamtengo wapatali.

    • Muyenera kutumiza limodzi ndi kalata yonena kuti zinthuzo ndi chopereka.

  • ZONGOBWEREKA

    • Mungapereke ndalama n’kufotokoza kuti ngati nthawi ina mungazifune mudzaitanitsa.

    • Muyenera kutumiza limodzi ndi kalata yonena kuti ndalamazo ndi zongobwereka.

  • MPHATSO ZINA

    Kuwonjezera pa kupereka mphatso za ndalama kapena zinthu zina zamtengo wapatali, pali njira zinanso zoperekera zinthu zothandiza pa ntchito ya Ufumu padziko lonse. Njira zimenezi zili m’munsimu. Musanasankhe njira iliyonse, muyenera kufunsa ku ofesi ya nthambi kuti mudziwe njira zimene ndi zotheka m’dziko lanu. Popeza malamulo amasiyana malinga ndi dziko, muyenera kufunsanso anthu odziwa bwino za malamulo ndiponso misonkho.

    Inshulansi: Mungakonze zoti gulu la Yehova lidzalandire ndalama za inshulansi kapena za penshoni.

    Maakaunti Akubanki: Mukhoza kupereka zinthu monga maakaunti anu akubanki, zikalata zosungitsira ndalama, kapena maakaunti a ndalama zimene mukusunga kuti mudzagwiritse ntchito mukadzapuma pa ntchito. Mukhozanso kukonza zoti mukadzamwalira, gululi lidzatenge zinthuzi. Pochita zimenezi, mutsatire malamulo amene mabanki a m’dziko lanu amayendera.

    Masheya: Mungapereke ku gulu la Yehova masheya amene muli nawo m’kampani kapena kukonza zoti lidzalandire masheyawo mukadzamwalira.

    Malo ndi Nyumba: Mungapereke ku gulu la Yehova malo ndi nyumba zoti zingagulitsidwe. Ngati ili nyumba yoti mukukhalamo, mukhoza kuipereka komabe n’kupitiriza kukhalamo pa nthawi yonse imene muli ndi moyo.

    Chuma Chamasiye: Mukhoza kulemba mu wilo yovomerezeka ndi boma kuti gulu la Yehova lidzapatsidwe katundu wanu kapena ndalama zanu, ngati inuyo mutamwalira.

Ngati mukufuna kudziwa zambiri za mmene mungaperekere mphatso zimenezi, lankhulani ndi a ku Accounting Office pa telefoni kapena alembereni kalata pa adiresi imene ili pansipa. Apo ayi, mungalembe kalata ku ofesi ya nthambi ya Mboni za Yehova ya m’dziko lanu.

ACCOUNTING OFFICE

Association of Jehovah’s Witnesses of Malawi

P.O. Box 30749

Lilongwe 3

Malawi

Telefoni: 01 762111

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena