Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 1/03 tsamba 3
  • Bokosi la Mafunso

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Bokosi la Mafunso
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Nkhani Yofanana
  • Phunziro la Baibulo la Mpingo ndi Msonkhano wa Utumiki Zasintha
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2012
  • Ndandanda Yatsopano ya Misonkhano ya Mpingo
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Lowani mu Mpumulo wa Mulungu
    Pulogalamu ya Msonkhano Wadera Wokhala ndi Woimira Nthambi wa 2023-2024
  • Muzikonda Yehova Ndi Mtima Wanu Wonse
    Pulogalamu ya Msonkhano Wadera wa 2019-2020​—Wokhala ndi Woimira Nthambi
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
km 1/03 tsamba 3

Bokosi la Mafunso

◼ Kodi ndani ayenera kupereka zilengezo pa Msonkhano wa Utumiki?

Cholinga cha mbali imeneyi ya Msonkhano wa Utumiki ndicho kudziŵitsa mpingo zinthu zofunika pa utumiki wathu. Zilengezo zina zimakhala zongotikumbutsa zina ndi zina ndipo zimakhala zofanana mlungu ndi mlungu. Komabe, zilengezo zonse ziyenera kuŵerengedwa momveka bwino, ndipo si ziyenera kuperekedwa mosaikirapo mtima kapena mwamwambo.

Malinga ndi mmene zilengezo zina zimakhalira, zingafunike mkulu kuzipereka. Zikatere, umakhala udindo wa woyang’anira wotsogolera kukonza zoti mkulu woyenerera azipereke, ndipo mbale wina apereke zilengezo zina zimene zakonzedwa.

Ngati kalata imene ili ndi nkhani yokhudza mpingo ilinso ndi nkhani ina yokhudza akulu okha, mkulu ndiye ayenera kuŵerenga nkhani yokhudza mpingoyo. Makalata ena ochokera ku ofesi ya nthambi amene amakhala ndi malangizo a mpingo angakhale bwino atamaŵerengedwa ndi mkulu woyenerera. Makalata ngati amenewo angakhale okhudza ntchito yapadera yolemba makalata okhudza abale athu amene akuzunzidwa. Makalata ena angakhale ndi mfundo zambiri zokhudza zimene zimachitika m’gulu lathu monga maulendo a oyang’anira madera ndi misonkhano ikuluikulu.

Nthaŵi zina pangafunike kupereka chilengezo chofunika kwambiri chokhudza thanzi la mpingo, ndipo chilengezocho chiyenera kuperekedwa momveka bwino. Zingakhale bwino ngati zilengezo zotero zitamaperekedwa ndi mkulu.

Kaya olengezawo ndi akulu kapena atumiki otumikira, zilengezozo ziyenera kukhala zomveka bwino komanso zachidule. Kutsata mfundo zimenezi kudzathandiza kuti malangizo opita ku mpingo azimveka bwino ndi kuti onse azipita patsogolo mogwirizana.—Sal. 133:1; 1 Akor. 14:8, 9, 40.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena