Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 8/02 tsamba 1
  • Pulogalamu Yatsopano ya Tsiku la Msonkhano Wapadera

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Pulogalamu Yatsopano ya Tsiku la Msonkhano Wapadera
  • Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • Nkhani Yofanana
  • Pulogalamu Yatsopano ya Tsiku la Msonkhano Wapadera
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
  • Pulogalamu Yatsopano ya Tsiku la Msonkhano Wapadera
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Pulogalamu ya Tsiku la Msonkhano Wapadera wa 2010
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Programu Yatsopano ya Tsiku la Msonkhano Wapadera
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
Onani Zambiri
Utumiki wathu wa Ufumu—2002
km 8/02 tsamba 1

Pulogalamu Yatsopano ya Tsiku la Msonkhano Wapadera

1 Manyuzipepala, ma TV, kapena mawailesi ndi aphunzitsi kusukulu amalimbikitsa kwambiri kukhala olemera mwakuthupi, koma Mawu a Mulungu amatilimbikitsa “Kukhala Olemera mu Ntchito Zabwino.” (1 Tim. 6:18, NW) Umenewu ndiwo mutu wa pulogalamu ya tsiku la msonkhano wapadera kuyambira mu September 2002. Kodi tikaphunzira zotani ku msonkhano umenewu?

2 Woyang’anira dera akafotokoza zimene zimafunika kuti “Tikhale Anthu Amene Mulungu Amati ndi Olemera,” ndipo adzafunsa anthu ena amene akuyesetsa kupeza chuma chauzimu. Mlendo amene adzakamba nkhani pamsonkhanowu adzasonyeza mu nkhani yake yoyamba momwe anthu a Mulungu akuchitira “Ntchito Zabwino mu Nthaŵi Yotuta Ino.” Tonse tikalimbikitsidwa kuona momwe tingathandizire kwambiri mu ntchito yotuta ya Mulungu, imene ikuchitika masiku ano.

3 Timasangalala kwambiri kuona achinyamata achikristu akufunafuna chuma chauzimu! Zimenezi zimalemekeza Yehova ndipo zimathandiza achinyamata kuyala maziko abwino kuti adzapeze mwayi wa mautumiki ena m’tsogolo muno. Mbali yakuti “Kuyamikira Achinyamata Chifukwa cha Ntchito Zabwino Potamanda Yehova” idzaunika ntchito zabwino zimene achinyamata achikristu a m’deralo akhala akuchita.

4 Kodi chingachitike n’chiyani ngati tichita ntchito zabwino? Mlendo adzakamba zimenezi mu nkhani yake yomaliza yakuti, “Pitirizani Kuchita Ntchito Zabwino Kuti Yehova Akudalitseni.” Adzakamba mbali zinayi zimene tingapeze madalitso ochuluka: (1) patokha, (2) monga banja, (3) monga mpingo, ndipo (4) monga gulu la padziko lonse.

5 Amene anadzipatulira kwa Yehova adzakhala ndi mwayi wobatizidwa. Ngati mwakonzeka kuchita zimenezi, uzani mwamsanga woyang’anira wotsogolera wanu.

6 Akalengeza tsiku la msonkhanowu kwanuko, fulumirani kukonzekera kuti mudzapezekepo. Yesetsani kufika mofulumira kuti mukaimbe nawo nyimbo yotsegulira ndiponso mukapemphere nawo. Kupezeka ndi kumvetsera mwatcheru pulogalamu yonse ya tsiku la msonkhano wapadera kudzatilimbikitsa kupitiriza kuyenda m’njira imene imatipangitsa kukhala anthu amene Mulungu wathu, Yehova amawaona kukhala olemeradi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena