Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 12/14 tsamba 6
  • Tizichitira Ena “Zabwino” Pokhala Ochereza (Mat. 12:35a)

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Tizichitira Ena “Zabwino” Pokhala Ochereza (Mat. 12:35a)
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Nkhani Yofanana
  • Kuchereza Alendo Ndi Kofunika Kwambiri
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2018
  • ‘Cherezani Alendo’
    Nsanja ya Olonda—1996
  • Kuchereza Alendo Kwachikristu m’Dziko Logaŵanikana
    Nsanja ya Olonda—1996
  • “Mucherezane Wina ndi Mnzake”
    Nsanja ya Olonda—2005
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
km 12/14 tsamba 6

Tizichitira Ena “Zabwino” Pokhala Ochereza (Mat. 12:35a)

N’zosakayikitsa kuti aliyense amafuna kuchitira ena “zabwino” ‘pokhala wochereza.’ (Aroma 12:13) Mwachitsanzo, akulu amalimbikitsidwa kuti azipereka chitsanzo chabwino pa nkhani yocherezayi. Angachite zimenezi poonetsetsa kuti omwe abwera kudzakamba nkhani ku mpingo kwawo akonzeredwa chakudya komanso ndalama zoyendera. Amawaitana kunyumba kwawo komanso kuwapatsa ndalama zoyendera. Komabe, nthawi zina tingaone ngati sitingakwanitse kuchereza poganiza kuti tilibe zowapatsa. Kapena tingamachite mantha kulandira alendo kunyumba kwathu. Koma mawu amene Yesu anauza Marita angatithandize kuti tisamaope kulandira alendo. (Luka 10:39-42) Yesu ananena kuti “chinthu chabwino kwambiri” munthu akalandira alendo ndi kucheza komanso kulimbikitsana nawo, osati kuwakonzera chakudya chapamwamba kapena kukhala ndi nyumba yokongoletsedwa bwino. Kuchita zimenezi kungatithandize kuti tizichitira abale ndi alongo athu zinthu “zabwino” mogwirizana ndi zimene Mawu a Mulungu amanena.—3 Yoh. 5-8.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena