Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb23 May tsamba 3
  • Muzidziona Mmene Yehova Amakuonerani

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzidziona Mmene Yehova Amakuonerani
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Nkhani Yofanana
  • Zosankha Zomwe Zimasonyeza Kuti Timadalira Yehova
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Tizivomereza Modzichepetsa Kuti Sitikudziwa Zonse
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
  • Musamakayikire Kuti Yehova Amakukondani
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
  • Yehova “Amachiritsa Anthu Osweka Mtima”
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2024
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
mwb23 May tsamba 3

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Muzidziona Mmene Yehova Amakuonerani

“Yehova amasangalala ndi anthu ake.” (Sl 149:4) Ngakhale kuti siife angwiro, iye amaona makhalidwe athu abwino komanso zomwe tingakwanitse kuchita. Komabe, nthawi zina zikhoza kutivuta kumadziona moyenera. Tikhoza kumamva ngati ndife osafunika chifukwa cha zimene ena amatichitira. Kapena, titamangoganizira zimene tinalakwitsa m’mbuyomu, tikhoza kumakayikira ngati Yehova angatikondedi. Ndiye kodi n’chiyani chingatithandize tikamamva chonchi?

Tizikumbukira kuti Yehova amaona zambiri kuposa zimene anthu amaona. (1Sa 16:7) Zimenezi zikutanthauza kuti iye amaona zambiri mwa ife kuposa mmene timadzionera. N’zosangalatsa kuti Baibulo limatithandiza kumvetsa mmene Yehova amationera. Tingamvetse zimenezi tikamawerenga nkhani za m’Baibulo zomwe zimasonyeza mmene Yehova amakondera anthu amene amamulambira.

ONERANI VIDIYO YAKUTI TSIMIKIZIRANI MTIMA WANU KUTI YEHOVA SAKUKUIMBANI MLANDU, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi fanizo la munthu wothamanga komanso bambo ake likutiphunzitsa chiyani zokhudza mmene Yehova amationera?

  • Ngati munthu amene anachita tchimo wachita zonse zofunika kuti akonzenso ubwenzi wake ndi Yehova, kodi angatsimikizire bwanji mtima wake kuti Yehova sakumuimba mlandu?​—1Yo 3:19, 20

  • Kodi kuwerenga komanso kuganizira mozama nkhani ya Davide ndi Yehosafati kunathandiza bwanji m’baleyu?

Nkhani za m’Baibulo zomwe zimatitsimikizira kuti . . .

Yehova amatikonda posatengera mmene ena amationera

  • Inoki (Ge 5:24; Ahe 11:5; Yuda 14, 15)

  • Hana (1Sa 1:1–2:11, 18-21, 26)

Yehova amakhululukira ndi mtima wonse anthu ochimwa omwe analapa

  • Manase (2Mb 33:1-7, 12, 13)

  • Paulo (1Ti 1:12-16)

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena