13 Ine ndapatsa munthu mphamvu kuti achitepo kanthu mwachilungamo,+
Ndipo njira zake zonse ndidzaziwongola.
Iye ndi amene adzamange mzinda wanga+
Komanso kumasula anthu anga amene ali ku ukapolo,+ popanda malipiro kapena chiphuphu,”+ akutero Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.