26 Ndiyeno anawauza kuti: “Ngati mudzamveradi mawu a Yehova Mulungu wanu, ndi kuchita zinthu zoyenera pamaso pake ndiponso kumvera malamulo ake ndi kusunga malangizo ake onse,+ sindidzakugwetserani miliri iliyonse imene ndinagwetsera Iguputo,+ chifukwa ine ndine Yehova amene ndikukuchiritsani.”+