Lachinayi, September 18
Nthawi zonse tizitamanda Mulungu. . . . Kuchita zimenezi kuli ngati nsembe imene tikupereka kwa Mulungu ndipo timagwiritsa ntchito milomo yathu polengeza dzina lake.—Aheb. 13:15.
Masiku ano Akhristu onse ali ndi mwayi wopereka nsembe kwa Yehova pogwiritsa ntchito nthawi, mphamvu ndiponso zinthu zawo pomutumikira. Tingasonyeze kuti timayamikira mwayi wathu wolambira Yehova poyesetsa kuchita zonse zomwe tingathe pomutumikira. Mtumwi Paulo anatchula zinthu zosiyanasiyana zokhudza kulambira kwathu zimene sitiyenera kuzinyalanyaza. (Aheb. 10:22-25) Zinthu zake zikuphatikizapo kupemphera kwa Yehova, kulengeza poyera chiyembekezo chathu, kusonkhana pamodzi ngati mpingo ndiponso kulimbikitsana, ‘makamaka panopa pamene tikuona kuti tsiku la [Yehova] likuyandikira.’ Pofuna kutsindika, chakumapeto kwa buku la Chivumbulutso, mngelo wa Yehova ananena kawiri kuti: “Lambira Mulungu.” (Chiv. 19:10; 22:9) Tiyeni tizikumbukira nthawi zonse mfundo zozama za choonadi zokhudza kachisi wamkulu wauzimu ndipo tiziyamikira mwayi wolambira Mulungu wathu wamkulu, Yehova. w23.10 29 ¶17-18
Lachisanu, September 19
Tiyeni tipitirize kukondana.—1 Yoh. 4:7.
Tonsefe tiyenera ‘kupitiriza kukondana.’ Koma tiyenera kukumbukira kuti Yesu anachenjeza kuti “chikondi cha anthu ambiri chidzazirala.” (Mat. 24:12) Yesu sankatanthauza kuti chikondi cha ophunzira ake ambiri chidzachepa. Ngakhale zili choncho, tiyenera kukhala osamala kuti tisatengere mtima wopanda chikondi womwe ndi wofala m’dzikoli. Poganizira mfundo imeneyi, tiyeni tikambirane funso lina lofunika. Kodi pali njira yodziwira ngati timakonda kwambiri abale athu? Njira imodzi yodziwira ngati timakonda kwambiri abale athu ndi kuona zimene timachita pa moyo wathu. (2 Akor. 8:8) Mtumwi Petulo anatchula chimodzi mwa zinthuzi pomwe anati: “Koposa zonse, muzikondana kwambiri chifukwa chikondi chimakwirira machimo ochuluka.” (1 Pet. 4:8) Choncho zimene timachita abale athu akalakwitsa zinthu, zingasonyeze ngati timawakonda kwambiri kapena ayi. w23.11 10-11 ¶12-13
Loweruka, September 20
Muzikondana.—Yoh. 13:34.
Sitingamvere lamulo la Yesu lakuti tizikondana ngati timakonda ena mumpingo n’kumalephera kukonda ena. N’zoona kuti tingamagwirizane kwambiri ndi ena kuposa ena, ngati mmenenso Yesu ankachitira. (Yoh. 13:23; 20:2) Koma mtumwi Petulo akutikumbutsa kuti tiyenera kuyesetsa kuti ‘tizikonda abale’ onse ngati anthu a m’banja lathu. (1 Pet. 2:17) Petulo anatilimbikitsa kuti ‘tizikondana kwambiri kuchokera mumtima.’ (1 Pet. 1:22) Apa mawu akuti ‘kukondana kwambiri’ akutanthauza kukonda winawake ngakhale pamene zili zovuta kutero. Mwachitsanzo, bwanji ngati m’bale watikhumudwitsa m’njira inayake? Mwachibadwa timafuna kumubwezera osati kumusonyeza chikondi. Komatu Petulo anaphunzira kwa Yesu kuti kubwezera sikusangalatsa Mulungu. (Yoh. 18:10, 11) Iye analemba kuti: “Munthu akakuchitirani choipa musamabwezere ndi choipa, akakuchitirani chipongwe musamabwezere ndi chipongwe. M’malomwake muziwachitira zabwino.” (1 Pet. 3:9) Muzilola kuti kukonda kwambiri ena, kuzikulimbikitsani kuti muzikomera mtima komanso kuganizira ena. w23.09 28-29 ¶9-11