Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mlungu Uno
September 22-28
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—2025 | September

SEPTEMBER 22-28

MLALIKI 1-2

Nyimbo Na. 103 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Pitirizani Kuphunzitsa M’badwo Wotsatira

(10 min.)

[Onerani VIDIYO yakuti Mfundo Zothandiza Kumvetsa Buku la Mlaliki.]

M’badwo uliwonse umakhala ndi udindo wophunzitsa m’badwo wotsatira (Mla 1:4; w17.01 27-28 ¶3-4)

Tikamaphunzitsa komanso kupatsa ena zochita, timawathandiza kuti nawonso azisangalala chifukwa chogwira ntchito mwakhama potumikira Yehova (Mla 2:24)

M’bale wachinyamata akuchititsa Phunziro la “Nsanja ya Olonda” ndipo m’bale wachikulire yemwe akuwerenga ndime, akumumwetulira.

Musamalephere kuphunzitsa abale achinyamata chifukwa choopa kuti adzakulandani maudindo amene mumasangalala nawo

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Mla 1:1—Kodi Baibulo limatanthauza chiyani likamanena kuti Solomo anali “wosonkhanitsa”? (it “Mlaliki” ¶1)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Mla 1:1-18 (th phunziro 11)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(2 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Pezani nkhani yomwe ingamusangalatse. Konzani zoti mudzalankhulanenso. (lmd phunziro 3 mfundo 5)

5. Ulendo Woyamba

(2 min.) KULALIKIRA M’MALO OPEZEKA ANTHU AMBIRI. Kambiranani nkhani imodzi yopezeka pagawo lakuti “Choonadi Chomwe Timakonda Kuphunzitsa Anthu” pogwiritsa ntchito njira yofotokozedwa mu zakumapeto A, m’kabuku kakuti Muzikonda Anthu—Muziwaphunzitsa. (lmd phunziro 2 mfundo 3)

6. Ulendo Wobwereza

(2 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Yankhani funso limene mwininyumba anafunsa pa ulendo wapita. (lmd phunziro 9 mfundo 5)

7. Kuphunzitsa Anthu

(5 min.) KULALIKIRA M’MALO OPEZEKA ANTHU AMBIRI. Musonyezeni mmene phunziro la Baibulo limachitikira, ndipo konzani zoti mudzapitirize ulendo wina. (lmd phunziro 10 mfundo 3)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 84

8. Mfundo Zitatu Zofunika pa Nkhani Yophunzitsa Ena

(15 min.) Nkhani yokambirana.

Zithunzi zosonyeza abale akuphunzitsa ena mu zochitika zosiyanasiyana. 1. M’bale akuphunzitsa mlongo mmene angagwiritsire ntchito chodulira matabwa pa malo a zomangamanga. 2. M’bale wachikulire akumvetsera pamene m’bale wachinyamata akuyeserera nkhani yake m’Nyumba ya Ufumu imene mulibe anthu. M’bale wachikulireyo ali ndi kabuku kakuti “Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso.” 3. M’bale akuphunzitsa wachinyamata mmene angaikire mabatire mu maikolofoni. 4. Bambo ndi ana ake awiri akuthandiza nawo kuyeretsa m’Nyumba ya Ufumu. Bamboyo ndi mwana wake wamkulu akusesa papulatifomu pamene mwana wake wamng’ono akupukuta sitandi yokambira nkhani.

Chikondi chimatilimbikitsa kuphunzitsa ena n’cholinga choti tikwanitse kugwira ntchito imene Yehova anatipatsa

M’Baibulo muli zitsanzo zabwino zambiri zomwe zimatithandiza kudziwa zimene tingachite pa nkhani yophunzitsa ena. Tingaphunzire zambiri tikaona mmene Samueli anaphunzitsira Sauli, mmene Eliya anaphunzitsira Elisa, mmene Yesu anaphunzitsira ophunzira ake komanso mmene Paulo anaphunzitsira Timoteyo. Koma Yehova ndi amene ali mphunzitsi wabwino kwambiri kuposa aliyense. Kodi tingaphunzire chiyani kuchokera pa chitsanzo chake?

Onerani VIDIYO yakuti Muzitsanzira Yehova pa Nkhani Yophunzitsa Ena (Yoh 5:20)—Kachigawo Kake. Kenako funsani funso ili:

  • Kodi ndi zinthu zitatu ziti zimene tingaphunzire kwa Yehova tikaona mmene amaphunzitsira ena?

9. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) lfb mutu 20-21

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 148 ndi Pemphero

Zimene Zili M’magaziniyi
Nsanja ya Olonda (Yophunzira)—2025 | July

Nkhani Yophunzira 29: September 22-28, 2025

8 Zimene Tingachite Kuti Tizipereka Malangizo Abwino

Nkhani Zina

Nkhani zina za m'magaziniyi

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena