Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w25 June tsamba 32
  • Zimene Zingakuthandizeni Kuti Muzikumbukira Malemba

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zimene Zingakuthandizeni Kuti Muzikumbukira Malemba
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
  • Nkhani Yofanana
  • Kugwiritsa Ntchito Baibulo Mwaluso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Kulozera Maganizo a Omvetsera ku Baibulo
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • Mmene Tingagwiritsire Ntchito Laibulale ya JW
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Kugwiritsa Ntchito Malemba Moyenerera
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
w25 June tsamba 32

MFUNDO ZOTHANDIZA POPHUNZIRA

Zimene Zingakuthandizeni Kuti Muzikumbukira Malemba

Kodi nthawi zina zimakuvutani kukumbukira lemba limene mumalikonda? Likhoza kukhala lemba limene limakulimbikitsani, limakuthandizani kupewa maganizo olakwika kapenanso limene mukufuna kufotokozera mnzanu. (Sal. 119:11, 111) Tiyeni tione zina zimene zingakuthandizeni kuti muzikumbukira malemba.

  • Muzigwiritsa ntchito matagi mu JW Library®. Mukhoza kukonza tagi n’kuilemba kuti “Malemba Amene Ndimakonda,” ndipo muzisungako malemba amene mukufuna muziwakumbukira.

  • Muzisunga malemba pamalo omwe mungathe kuwaona. Muzilemba papepala vesi limene mukufuna muzilikumbukira ndipo muziliika pamalo omwe mungathe kuliona mosavuta. Ena amaika pagalasi kapena pafiliji, pomwe ena amajambula lembalo n’kuliika ngati chithunzi kuti lizionekera akatsegula foni kapena kompyuta yawo.

  • Muzigwiritsa ntchito makadi. Muzilemba vesilo mbali ina n’kulemba mawu ake kuseri kwake. Kenako muziyesa kuona lembalo n’kutchula mawu ake kapena kuona mawuwo n’kutchula lemba lake.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena