LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • Macitidwe 5
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la Macitidwe

      • Hananiya ndi Safira (1-11)

      • Atumwi acita zizindikilo zambili (12-16)

      • Amangidwa kenako amasulidwa (17-21a)

      • Apelekedwanso ku Khoti Yaikulu ya Ayuda (21b-32)

        • ‘Kumvela Mulungu osati anthu’ (29)

      • Ulangizi wa Gamaliyeli (33-40)

      • Kulalikila kunyumba ndi nyumba (41, 42)

Macitidwe 5:18

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “n’kumanga.”

Macitidwe 5:21

Mawu amunsi

  • *

    M’cinenelo coyambilila, “Sanihedirini.”

Macitidwe 5:22

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    3/2020, tsa. 31

Macitidwe 5:26

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    3/2020, tsa. 31

Macitidwe 5:28

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 21

Macitidwe 5:29

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 21

Macitidwe 5:33

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “analasidwa mtima.”

Macitidwe 5:38

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 21

Macitidwe 5:39

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 21

Macitidwe 5:40

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “n’kuwamenya.”

Macitidwe 5:41

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Ufumu wa Mulungu Ukulamulila, tsa. 135

Macitidwe 5:42

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 18

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
  • 31
  • 32
  • 33
  • 34
  • 35
  • 36
  • 37
  • 38
  • 39
  • 40
  • 41
  • 42
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
Macitidwe 5:1-42

Macitidwe a Atumwi

5 Tsopano munthu wina, dzina lake Hananiya, ndi mkazi wake Safira, anagulitsa munda wawo. 2 Koma mwamseli iye anacotsapo ndalama zina ndipo mkazi wake anadziwa. Ndalama zotsalazo anazipeleka kwa atumwi. 3 Koma Petulo anati: “Hananiya, n’cifukwa ciyani Satana wakulimbitsa mtima kuti unamize mzimu woyela n’kubisa ndalama zina za mundawo? 4 Mundawo usanaugulitse, kodi sunali wako? Ndipo utaugulitsa, ndalama zake sukanacita nazo zimene unali kufuna? N’cifukwa ciyani unaganiza zocita zimenezi mumtima mwako? Sunanamize anthu koma wanamiza Mulungu.” 5 Hananiya atamva mawu amenewa anangoti pansi khu! n’kumwalila. Ndipo onse amene anamva za nkhaniyi anacita mantha kwambili. 6 Ndiyeno anyamata anabwela n’kukulunga thupi lake mu nsalu kenako anatuluka naye n’kukamuika m’manda.

7 Ndiyeno patapita maola pafupifupi atatu mkazi wake analowa ndipo sanadziwe zimene zinacitika. 8 Petulo anamufunsa kuti: “Ndiuze, kodi ndalama zonse zimene awilinu munagulitsa munda uja ndi izi?” Iye anati: “Inde, ndi zimenezi.” 9 Kenako Petulo anamufunsa kuti: “N’cifukwa ciyani inu awili munagwilizana zakuti muyese mzimu wa Yehova? Taona, mapazi a anthu amene aika mwamuna wako m’manda ali pakhomo. Iwenso akunyamula n’kutuluka nawe.” 10 Nthawi yomweyo iye anangoti pansi khu! kumapazi a Petulo n’kufa. Pamene anyamata aja amalowa anapeza kuti wafa kale. Iwo anamunyamula n’kutuluka naye, ndipo anapita kukamuika m’manda pafupi ndi mwamuna wake. 11 Conco mpingo wonse komanso anthu onse amene anamva zimenezi, anacita mantha kwambili.

12 Komanso atumwi anapitiliza kucita zizindikilo ndi zodabwitsa zambili pakati pa anthu. Ndipo onse okhulupilila anali kusonkhana pa Khonde la Zipilala la Solomo. 13 Kukamba zoona, panalibe ndi mmodzi yemwe mwa enawo amene analimba mtima kugwilizana ndi ophunzilawo, koma anthu anali kuwatamanda. 14 Kuposa pamenepo, okhulupilila Ambuye anapitiliza kuwonjezeka cifukwa amuna ndi akazi ambili anakhala okhulupilila. 15 Iwo anali kubweletsa anthu odwala m’misewu n’kuwagoneka pa timabedi komanso pa mphasa kuti Petulo akadutsa, cithunzithunzi cake cokha cifike pa ena a iwo. 16 Ndiponso makamu a anthu ocokela ku mizinda yozungulila Yerusalemu anali kupita kumeneko, atanyamula anthu odwala komanso amene anali kuzunzika ndi mizimu yonyansa. Ndipo onsewo anacilitsidwa.

17 Koma mkulu wa ansembe pamodzi ndi onse amene anali naye, amene anali a gulu la mpatuko la Asaduki, anacita nsanje. 18 Conco iwo ananyamuka n’kugwila* atumwiwo, ndipo anawaponya m’ndende ya mumzindawo. 19 Koma usiku, mngelo wa Yehova anatsegula zitseko za ndendeyo n’kuwatulutsa, ndipo anawauza kuti: 20 “Pitani mukaimilile m’kacisi, ndipo mupitilize kuuza anthu zokhudza moyo umene ukubwelawo.” 21 Atamva zimenezi, iwo analowa m’kacisi m’mamawa kwambili n’kuyamba kuphunzitsa.

Tsopano mkulu wa ansembe ndi onse amene anali nawo atafika, anasonkhanitsa a m’Bungwe Lalikulu la Ayuda* komanso akulu onse a Aisiraeli. Kenako anatuma alonda a ku ndende kuti akatenge atumwiwo n’kuwabweletsa kwa iwo. 22 Koma alondawo atafika kumeneko sanawapeze m’ndendemo. Conco iwo anabwelela kuti akawafotokozele zimenezi. 23 Iwo anati: “Ife tapeza kuti ndende ndi yokhoma ndiponso ndi yotetezedwa bwino, ndipo alonda anali cilili m’makomo. Koma titatsegula tapeza kuti mkati mulibe aliyense.” 24 Akapitawo a pakacisi komanso ansembe aakulu atamva zimenezi anathedwa nzelu, cifukwa sanadziwe kuti nkhaniyi idzatha bwanji. 25 Koma kunabwela munthu wina, ndipo anawauza kuti: “Anthu inu! Amuna aja amene munawaika m’ndende ali m’kacisi aimilila mmenemo ndipo akuphunzitsa anthu.” 26 Ndiyeno kapitawo wa pakacisi uja ndi alonda ake anapita kukawatenga. Koma osati mwaciwawa cifukwa iwo anali kuopa kuti anthu angawaponye miyala.

27 Conco anawabweletsa n’kuwaimilika pamaso pa Bungwe Lalikulu la Ayuda. Kenako mkulu wa ansembe ananena 28 kuti: “Tinakulamulani mwamphamvu kuti musapitilize kuphunzitsa m’dzina limeneli, koma taonani mwadzaza Yerusalemu yense ndi zimene mukuphunzitsa, ndipo mwatsimikiza mtima kubweletsa magazi a munthu uyu pa ife.” 29 Poyankha, Petulo ndi atumwi enawo anati: “Ife tiyenela kumvela Mulungu monga wolamulila osati anthu. 30 Mulungu wa makolo athu akale anaukitsa Yesu, amene inu munamupha mwa kumupacika pamtengo. 31 Mulungu anamukweza kudzanja lake lamanja monga Mtumiki wake Wamkulu ndi Mpulumutsi, kuti Aisiraeli alape komanso kuti akhululukidwe macimo awo. 32 Ndipo ife ndife mboni za zinthu zimenezi. Mzimu woyela umene Mulungu waupeleka kwa anthu amene amamumvela monga wolamulila wawo, nawonso ndi mboni.”

33 Iwo atamva zimenezi anakwiya* kwambili moti anafuna kuwapha. 34 Koma Mfarisi wina dzina lake Gamaliyeli anaimilila m’Bungwe Lalikulu la Ayuda. Iye anali mphunzitsi wa Cilamulo amene anthu onse anali kumulemekeza, ndipo analamula kuti amunawo atulutsidwe panja kwakanthawi. 35 Kenako anawauza kuti: “Amuna inu Aisiraeli, samalani ndi zimene mukufuna kuwacita anthuwa. 36 Mwacitsanzo, m’masiku akumbuyoku, kunali Teuda amene anadzichukitsa kwambili, ndipo amuna pafupifupi 400 analowa m’gulu lake. Koma iye anaphedwa, ndipo onse amene anali kumutsatila anamwazikana moti sanapezekenso. 37 Pambuyo pake kunabwela Yudasi Mgalileya m’masiku a kalembela. Iye anakopa anthu ambili ndipo anali kumutsatila. Koma nayenso anafa ndipo onse amene anali kumutsatila anamwazikana. 38 Conco malinga ndi mmene zinthu zilili apa, ndikukuuzani kuti musalimbane nawo anthu awa, koma alekeni. Cifukwa ngati pulani yawo kapena nchito yawo ndi yocokela kwa anthu sipita patali. 39 Koma ngati ndi yocokela kwa Mulungu, simungakwanitse kuwaletsa. Cifukwa mukapitiliza mudzapezeka kuti mukulimbana ndi Mulungu.” 40 Iwo anamvela malangizo ake, ndipo anaitana atumwiwo n’kuwakwapula* ndi kuwalamula kuti aleke kulankhula m’dzina la Yesu, ndipo anawamasula.

41 Conco atumwiwo, anacoka pamaso pa Bungwe Lalikulu la Ayuda ali osangalala cifukwa Mulungu anawaona kuti ndi oyenela kucititsidwa manyazi kaamba ka dzina la Yesu. 42 Ndipo tsiku ndi tsiku iwo anapitiliza kuphunzitsa mwakhama m’kacisi komanso kunyumba ndi nyumba, ndipo anali kulengeza uthenga wabwino wonena za Khristu Yesu.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani