Kalata Yopita kwa Akolose
4 Inu ambuye, muzicitila akapolo anu zinthu zacilungamo ndi zoyenela, popeza mukudziwa kuti inunso muli ndi Ambuye kumwamba.
2 Muzilimbikila kupemphela. Ndipo pa nkhani imeneyi mukhale maso ndipo muziyamikila. 3 Komanso muzitipemphelela kuti Mulungu atitsegulile khomo kuti tithe kulalikila mau ndi kulankhula za cinsinsi copatulika conena za Khristu, cimene andimangila muno m’ndende, 4 ndi kuti ndidzalalikila za cinsinsico momveka bwino monga mmene ndiyenela kucitila.
5 Muziyenda mwanzelu pocita zinthu ndi anthu akunja, ndipo muzigwilitsa nchito bwino nthawi yanu.* 6 Nthawi zonse mau anu azikhala okoma ngati kuti mwawathila mcele, kuti mudziwe mmene mungayankhile munthu aliyense.
7 Tukiko m’bale wanga wokondedwa, adzakuuzani zonse za ine. Iye ndi mtumiki wokhulupilika komanso kapolo mnzanga mwa Ambuye. 8 Ndikumutumiza kwa inu kuti mudziwe mmene tilili, komanso kuti adzalimbikitse mitima yanu. 9 Iye akubwela kwa inu limodzi ndi Onesimo m’bale wanga wokhulupilika ndi wokondedwa, amene anacokela pakati panu. Iwo adzakufotokozelani zonse zimene zikucitika kuno.
10 Arisitako mkaidi mnzanga akupeleka moni kwa nonsenu. Nayenso Maliko msuweni wa Baranaba, (amene ndinakulangizani kuti mumulandile nthawi iliyonse akadzafika kwa inu), 11 ndi Yesu wodziwikanso kuti Yusito, akuti moni. Iwo ali m’gulu la anthu odulidwa. Iwo okha ndi anchito anzanga pa za Ufumu wa Mulungu, ndipo amandilimbikitsa kwambili. 12 Epafura, amene anacokela pakati panu, amenenso ndi kapolo wa Khristu Yesu akuti moni. Iye amakupemphelelani mwakhama nthawi zonse kuti mupitilize kukhala olimba mwauzimu ndi osakaika ngakhale pang’ono za cifunilo conse ca Mulungu. 13 Ine ndikumucitila umboni kuti amadzipeleka kwambili cifukwa ca inu, komanso cifukwa ca abale a ku Laodikaya ndi ku Herapoli.
14 Luka, dokotala wokondedwa, komanso Dema akuti moni kwa nonsenu. 15 Mundipelekele moni kwa abale a ku Laodikaya komanso kwa Numfa ndi mpingo umene umasonkhana panyumba pake. 16 Mukaiwelenga kalatayi kwanuko, konzani zakuti ikawelengedwenso ku mpingo wa Alaodikaya. Inunso mukawelenge yocokela ku Laodikaya. 17 Komanso muuze Arikipo kuti: “Uonetsetse kuti utumiki umene unaulandila mwa Ambuye ukuukwanilitsa.”
18 Tsopano landilani moni umene ine Paulo ndalemba ndi dzanja langa. Pitilizani kukumbukila maunyolo anga kundende kuno. Cisomo ca Mulungu wathu cikhale nanu.