Uthenga Wabwino Wolembedwa ndi Yohane
3 Panali Mfarisi wina dzina lake Nikodemo, wolamulila wa Ayuda. 2 Munthu ameneyu anapita kwa Yesu usiku n’kumuuza kuti: “Rabi,* tikudziwa kuti ndinu mphunzitsi wocokela kwa Mulungu, cifukwa palibe munthu angakwanitse kucita zizindikilo zimene mumacita ngati Mulungu sali naye.” 3 Yesu anamuyankha kuti: “Ndithudi ndikukuuza, ngati munthu sanabadwenso,* n’zosatheka kuona Ufumu wa Mulungu.” 4 Nikodemo anamufunsa kuti: “Kodi munthu angabadwe bwanji ngati ndi wamkulu kale? Iye sangalowe m’mimba mwa mayi ake kaciwili n’kubadwanso, angatelo kodi?” 5 Yesu anayankha kuti: “Ndithudi ndikukuuza, ngati munthu sanabadwe mwa madzi ndi mzimu n’zosatheka iye kulowa mu Ufumu wa Mulungu. 6 Wobadwa kwa munthu ndi munthu, ndipo cobadwa ku mzimu ndi mzimu. 7 Usadabwe cifukwa ndakuuza kuti: Anthu inu muyenela kubadwanso. 8 Mphepo imakunthila kumene ikufuna, ndipo inu mumangomvako mkokomo wake, koma simumadziwa kumene yacokela ndi kumene ikupita. Ndi mmenenso zimakhalila kwa aliyense amene wabadwa mu mzimu.”
9 Nikodemo poyankha anati: “Kodi zimenezi zingatheke bwanji?” 10 Yesu anamufunsa kuti: “Kodi sikuti ndiwe mphunzitsi mu Isiraeli, ndiye zitheka bwanji kuti sudziwa zinthu zimenezi? 11 Ndithudi ndikukuuza, zimene tidziwa timazikamba, ndipo zimene taona timazicitila umboni. Koma inu simulandila umboni umene timakupatsani. 12 Ngati ndakuuzani zinthu za padziko lapansi koma simukhulupililabe, mungakhulupilile bwanji ndikakuuzani zinthu zakumwamba? 13 Ndiponso palibe munthu amene anakwelapo kumwamba koma Mwana wa munthu yekha, amene anatsika kucokela kumwambako. 14 Monga mmene Mose anakwezela njoka m’mwamba m’cipululu, nayenso Mwana wa munthu ayenela kukwezedwa m’mwamba, 15 kuti aliyense wokhulupilila iye akapeze moyo wosatha.
16 “Pakuti Mulungu analikonda kwambili dziko, moti anapeleka Mwana wake wobadwa yekha, kuti aliyense womukhulupilila asawonongeke, koma akapeze moyo wosatha. 17 Mulungu sanatumize Mwana wake m’dziko kuti adzaliweluze koma kuti dzikolo lipulumutsidwe kupitila mwa iye. 18 Munthu aliyense wokhulupilila mwa iye sayenela kuweluzidwa. Munthu aliyense wosamukhulupilila waweluzidwa kale, cifukwa sanakhulupilile* Mwana wobadwa yekha wa Mulungu. 19 Tsopano maziko a ciweluzo ndi awa: kuwala kwabwela m’dziko, koma anthu akonda mdima m’malo mwa kuwala, cifukwa ca nchito zawo zoipa. 20 Pakuti aliyense wocita zinthu zoipa amadana ndi kuwala, ndipo sabwela pomwe pali kuwala kuti nchito zake zisaonekele poyela.* 21 Koma amene amacita zabwino, amabwela pamene pali kuwala, kuti nchito zake zionekele kuti anazicita mogwilizana ndi cifunilo ca Mulungu.”
22 Zitatha izi, Yesu ndi ophunzila ake anapita kumadela akumidzi a ku Yudeya. Kumeneko anakhala nawo kwa kanthawi ndipo anali kubatiza anthu. 23 Koma nayenso Yohane anali kubatiza anthu ku Ainoni pafupi ndi Salimu, cifukwa kunali madzi ambili, ndipo anthu anali kupita kumeneko kukabatizidwa. 24 Pa nthawiyi n’kuti Yohane anali asanaponyedwe m’ndende.
25 Tsopano ophunzila a Yohane anakangana ndi Myuda wina pa nkhani ya kukhala woyela pamaso pa Mulungu. 26 Conco iwo anapita kwa Yohane n’kumuuza kuti: “Mphunzitsi,* munthu amene munali naye kutsidya la Yorodano, amenenso munamucitila umboni, onani, akubatiza anthu, ndipo onse akupita kwa iye.” 27 Yohane anayankha kuti: “Munthu sangalandile kanthu kalikonse ngati sanapatsidwe kucokela kumwamba. 28 Inuyo mungandicitile umboni kuti ndinati, ‘Ine sindine Khristu, koma ndinatumidwa kuti ndikhale kalambulabwalo wake.’ 29 Mwiniwake wa mkwatibwi ndi mkwati. Koma mnzake wa mkwati akaimilila n’kumva mawu a mkwatiyo, amakondwela kwambili. Conco ine ndine wokondwa kwambili. 30 Ameneyo ayenela kupitiliza kuwonjezeka, koma ine ndiyenela kumacepelacepela.”
31 Amene wacokela kumwamba amaposa ena onse. Amene wacokela pa dziko lapansi ndi wa padziko lapansi, ndipo amakamba zinthu za padziko lapansi. Amene wacokela kumwamba amaposa ena onse. 32 Iye amacitila umboni zimene waona ndi kumva, koma palibe munthu amene amakhulupilila umboni wake. 33 Aliyense amene wakhulupilila umboni wake, wauika cidindo* umboniwo kuti Mulungu ndi woona. 34 Pakuti amene Mulungu anamutuma, amanena mawu a Mulungu, cifukwa Iye sapeleka mzimu moumila.* 35 Atate amakonda Mwana, ndipo anapeleka zinthu zonse m’manja mwake. 36 Amene amakhulupilila Mwanayo adzapeza moyo wosatha. Amene samvela Mwanayo sadzauona moyowo, koma mkwiyo wa Mulungu udzakhalabe pa iye.