LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb17 April tsa. 6
  • Nyimbo za Ufumu Zimathandiza Kukhala Wolimba Mtima

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Nyimbo za Ufumu Zimathandiza Kukhala Wolimba Mtima
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Nkhani Zofanana
  • Muziimba Mosangalala Nyimbo Zotamanda Yehova
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
  • Mfundo Yothandiza pa Kuŵelenga Kwanu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2023
  • Nyimbo Zatsopano Zogwilitsila Nchito Polambila
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Nyimbo Zimene Zimatiyandikizitsa kwa Mulungu
    Mmene Zopeleka Zanu Zimagwilila Nchito
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
mwb17 April tsa. 6

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Nyimbo za Ufumu Zimathandiza Kukhala Wolimba Mtima

M’bale Erich Frost wakhala pafupi na piyano

Pamene Paulo na Sila anali m’ndende, anatamanda Mulungu ndi nyimbo. (Mac. 16:25) M’zaka zamakono, okhulupilila anzathu anali kuimba nyimbo za Ufumu m’ndende ya Sachsenhausen pa nthawi ya cipani ca Nazi ku Germany, ndiponso pamene anali m’ndende ku Siberia. Zitsanzozi zionetsa kuti nyimbo zimathandiza Akhristu kukhala olimba mtima panthawi ya mayeselo.

Posacedwa, tidzalandila buku la nyimbo zatsopano lakuti “Imbani mwa Cisangalalo” kwa Yehova. Tikadzalandila buku limeneli, tidzakhomeleze mau ake pamtima mwa kumaimba nyimbozo pa kulambila kwa pabanja. (Aef. 5:19) Tikatelo, mzimu woyela udzatithandiza kuzikumbukila nyimbozo panthawi ya mayeselo. Nyimbo za Ufumu zimatithandiza kusumika maganizo pa ciyembekezo cathu. Zimalimbikitsa ngako pamayeselo. Cina, pamene tili acimwemwe, mau otsitsimula a nyimbo amatithandiza ‘kuimba mwacisangalalo,’ cifukwa comvela bwino mumtima. (1 Mbiri 15:16; Sal. 33:1-3) Tiyeni tonse tikapindule nazo mokwanila nyimbo zathu za Ufumuzo.

TAMBANI VIDIYO YAKUTI NYIMBO IMENE INALIMBIKITSA AKAIDI. NDIYENO YANKHANI MAFUNSO AYA:

  • N’ciani cinacititsa M’bale Frost kupeka nyimbo?

  • Kodi nyimbo zinawathandiza bwanji abale m’ndende ya Sachsenhausen?

  • Ni pa zocitika za tsiku na tsiku ziti pamene nyimbo za Ufumu zingakulimbikitseni?

  • Ni nyimbo za Ufumu ziti zimene mungakonde kuziika pamtima?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani