LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w13 12/1 tsa. 32
  • Kuyankha Mafunso a M’baibo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kuyankha Mafunso a M’baibo
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
  • Nkhani Zofanana
  • Kuyankha Mafunso a M’baibo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
  • Kodi Yesu Adzacita Ciani Mtsogolo?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Kuyankha Mafunso a M’baibo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
  • Kodi Ufumu wa Mulungu N’ciani?
    Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
w13 12/1 tsa. 32

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBO

Kodi colinga ca kubwelanso kwa Kristu n’ciani?

Yesu Kristu asanapite kumwamba m’caka ca 33 C.E., analonjeza kuti adzabwelanso. Iye anadziyelekezela ndi munthu wa m’banja lacifumu amene anapita ku dziko lakutali ndipo atabwelako anakhala mfumu. Colinga ca kubwelanso kwa Yesu ndi kubweletsa boma labwino kwa anthu.—Ŵelengani Luka 19:11, 12.

Kodi Kristu adzabwela ndi thupi lotani? Iye anaukitsidwa ndi thupi lauzimu limene silioneka. (1 Petulo 3:18) Ndiyeno, Yesu anapita kumwamba ndi kukakhala kudzanja lamanja la Mulungu. (Salimo 110:1) Patapita zaka, anamubweletsa pafupi ndi “Wamasiku Ambili,” Yehova Mulungu, amene anapatsa Yesu mphamvu zolamulila anthu onse. Conco Yesu adzabwelanso monga Mfumu yosaoneka osati monga munthu.—Ŵelengani Danieli 7:13, 14.

Kodi Yesu adzacita ciani akadzabwela?

Yesu akadzabwela mosaoneka ndi angelo ake, adzaweluza anthu. Iye adzaononga anthu oipa koma adzapeleka moyo wosatha kwa anthu onse amene amamuvomeleza monga Mfumu.—Ŵelengani Mateyu 25:31-33, 46.

Pamene Yesu adzalamulila dziko lapansi monga Mfumu, adzalisandutsa kukhala paradaiso. Iye adzaukitsa akufa n’colinga cakuti akasangalale ndi moyo m’Paradaiso padziko lapansi.—Ŵelengani Luka 23:42, 43.

Kuti mudziŵe zambili, onani tsamba 73 mpaka 85 m’buku ili, Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni, lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Mungatenge buku limeneli pa www.jw.org

[Cithunzi papeji 32]

Yesu adzabweletsa boma labwino kwa anthu

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani