LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w14 4/1 masa. 16-32
  • Kodi Yesu Adzacita Ciani Mtsogolo?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Yesu Adzacita Ciani Mtsogolo?
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Nkhani Zofanana
  • Kuyankha Mafunso a m’Baibulo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Kuyankha Mafunso a M’baibo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
  • Kuyankha Mafunso a M’baibo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2013
  • Kuyankha Mafunso A m’Baibulo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
w14 4/1 masa. 16-32

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

Kodi Yesu adzacita ciani mtsogolo?

M’caka ca 33 C.E.,Yesu anaphedwa, ndipo anaukitsidwa ndi kupita kumwamba. Pambuyo pake, iye anaikidwa kukhala Mfumu. (Danieli 7:13, 14) Pokhala Mfumu, Yesu mtsogolo adzabweletsa mtendele padziko lapansi ndi kucotsapo njala.—Ŵelengani Salimo 72:7, 8, 13.

Pokhala Mfumu, Yesu adzacotsa kusalungama konse padziko lapansi

Monga Wolamulila wa anthu, Yesu adzacita zinthu zabwino zambili. Adzagwilitsila nchito mphamvu zimene Atate wake anam’patsa kubwezeletsa anthu ku ungwilo. Anthu adzasangalala ndi moyo padziko lapansi ndipo sadzakalamba ndi kufa.—Ŵelengani Yohane 5:26-29; 1 Akorinto 15:25, 26.

Kodi Yesu akucita ciani tsopano?

Yesu tsopano akutsogolela nchito yolalikila ya otsatila ake oona. Iwo amacezela anthu ndi kuwaonetsa zimene Baibulo limanena zokhudza Ufumu wa Mulungu. Yesu anakamba kuti adzapitiliza kucilikiza ophunzila ake mpaka pamene Ufumu wa Mulungu udzacotsapo maboma a anthu.—Ŵelengani Mateyu 24:14; 28:19, 20.

Mogwilitsila nchito mpingo woona wacikristu, Yesu akuthandiza anthu kukhala ndi umoyo wabwino. Adzapitilizabe kuwatsogolela mpaka pa cionongeko ca dongosolo ili la zinthu ndi kuwaloŵetsa m’dziko latsopano.—Ŵelengani 2 Petulo 3:7, 13; Chivumbulutso 7:17.

Kuti mudziŵe zambili, onani nkhani 8 m’buku ili Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni, lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Mungatenge buku limeneli www.jw.org

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani