LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb18 October tsa. 8
  • Akhristu Oona Amadziŵika na Cikondi—Kondwelani na Coonadi

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Akhristu Oona Amadziŵika na Cikondi—Kondwelani na Coonadi
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
  • Nkhani Zofanana
  • “Cikondi . . . Sicikondwela ndi Zosalungama”
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
  • Anthu a Yehova “Aleke Kucita Zosalungama”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Tsiku Loyamba
    Pulogilamu ya Msonkhano Wacigawo wa mu 2020
  • Mmene Tingaonetsele Cikondi kwa Anthu Anzathu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2020
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
mwb18 October tsa. 8

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Akhristu Oona Amadziŵika na Cikondi—Kondwelani na Coonadi

CIFUKWA CAKE N’KOFUNIKA: Potengela citsanzo ca Yesu, tifunika kucitila umboni coonadi cokamba za colinga ca Mulungu. (Yoh. 18:37) Tifunikanso kukondwela na coonadi, kumakamba zoona komanso kumaganizila zilizonse za zoona, olo kuti tikukhala m’dziko lodzala mabodza ndiponso limene limacita zosalungama.—1 Akor. 13:6; Afil. 4:8.

MMENE TINGACITILE:

  • Tsimikizani mtima kuti musamamvele kapena kufalitsa misece.—1 Ates. 4:11

  • Musamakondwele wina akamavutika

  • Muzikondwela na zinthu zabwino ndiponso zolimbikitsa

TAMBITSANI VIDIYO YAKUTI “MUZIKONDANA”—KONDWELANI NDI COONADI OSATI NDI ZOSALUNGAMA, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO OTSATILAWA:

  • Kodi mlongo Debbie “anakondwela ndi zosalungama” m’lingalilo lanji?

  • Nanga mlongo Alice anasintha bwanji makambilano awo na mlongo Debbie kuti akhale oyenela?

  • Ni zinthu zabwino ziti zimene tingakambilane?

Alice akamba na Debbie

Kondwelani na coonadi osati na zosalungama

CITSANZO CA M’BAIBO COFUNIKA KUCISINKHA-SINKHA: Loti anali kuzunzika kwambili mu mtima na khalidwe loipa la anthu a mu mzinda wa Sodomu na Gomora.—2 Pet. 2:8.

DZIFUNSENI KUTI, ‘Ningaonetse bwanji kuti nimakondwela na coonadi osati na zinthu zosalungama?’

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani