Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 17:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Chotero asamaperekenso nsembe zawo ku ziwanda zooneka ngati mbuzi*+ zimene akuchita nazo chiwerewere.+ Limeneli likhale lamulo kwa inu mpaka kalekale, m’mibadwo yanu yonse.”’

  • Deuteronomo 31:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Tsopano Yehova anauza Mose kuti: “Iweyo ugona pamodzi ndi makolo ako,+ ndipo anthu awa adzaimirira+ ndi kuchita chiwerewere pakati pawo ndi milungu yachilendo ya m’dziko limene akupita.+ Iwo adzandisiya+ ndi kuphwanya pangano limene ndinapangana nawo.+

  • Oweruza 2:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Ana a Isiraeli sanamvere ngakhale oweruza awo, koma anachita chiwerewere+ ndi milungu ina+ ndi kuigwadira. Iwo anapatuka mwamsanga panjira imene makolo awo anayendamo. Makolo awo anayenda m’njira imeneyo mwa kumvera malamulo a Yehova,+ koma iwo sanachite mofanana ndi makolo awo.

  • Oweruza 8:33
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 33 Ndiyeno zinachitika kuti Gidiyoni atangomwalira, ana a Isiraeli anayambanso kupembedza Abaala,+ moti anaika Baala-beriti* kukhala mulungu wawo.+

  • Yeremiya 3:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Iye anayamba kuchita uhule chifukwa choona nkhani imeneyi mopepuka. Anali kuipitsa dzikolo+ ndi kuchita chigololo ndi miyala komanso mitengo.+

  • Ezekieli 6:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Opulumuka anu akadzagwidwa n’kutengedwa kukakhala pakati pa mitundu ina ya anthu, ndithu adzandikumbukira.+ Adzakumbukira mmene ndinamvera kupweteka chifukwa cha mtima wawo wadama umene unawachititsa kundipandukira.+ Adzakumbukiranso mmene ndinamvera kupweteka chifukwa cha maso awo othamangira mafano awo onyansa pofuna kuchita nawo zadama.+ Iwo adzachita manyazi ochita kuonekera pankhope zawo, chifukwa cha zinthu zonse zoipa ndi zonyansa zimene anachita.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena