20 Yehova anapitiriza kulankhula ndi Aroni, kuti: “Iwe udzakhala wopanda cholowa m’dziko mwawo, ndipo sudzapatsidwa gawo lililonse pakati pawo.+ Ine ndine gawo lako ndi cholowa chako pakati pa ana a Isiraeli.+
62 Onse amene anawerengedwa pakati pa Alevi analipo 23,000. Amenewa anali amuna onse kuyambira amwezi umodzi kupita m’tsogolo.+ Iwowa sanawerengedwe limodzi ndi ana a Isiraeli,+ chifukwa sanafunikire kulandira cholowa pakati pa ana a Isiraeli.+