14 Kumadzulo kwa gawolo, malirewo anakhotera kum’mwera, paphiri loyang’anizana ndi kum’mwera kwa Beti-horoni. Kuchokera pamenepo anakathera ku Kiriyati-baala, kutanthauza Kiriyati-yearimu,+ womwe ndi mzinda wa ana a Yuda. Awa ndiwo malire a kumadzulo a gawo la Benjamini.